< Zacharie 6 >

1 Et je me retournai, et je levai les yeux, et je regardai, et voilà quatre chars sortant entre deux montagnes, et ces montagnes étaient d'airain.
Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona magaleta anayi akutuluka pakati pa mapiri awiri, mapiri amkuwa.
2 Au premier char il y avait des chevaux roux, et au second char, des chevaux noirs,
Galeta loyamba limakokedwa ndi akavalo ofiira, lachiwiri ndi akavalo akuda,
3 et au troisième char, des chevaux blancs, et au quatrième char, des chevaux noirs.
lachitatu ndi akavalo oyera, ndipo lachinayi ndi akavalo otuwa a mawanga ofiirira, onsewa anali akavalo amphamvu kwambiri.
4 Et je parlai, et je dis à l'ange qui parlait avec moi: Qu'est cela, Seigneur?
Ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane uja kuti, “Kodi mbuye wanga chimenechi nʼchiyani?”
5 Et l'ange qui parlait avec moi me répondit, et me dit: Ce sont les quatre vents du ciel; ils sortent pour se tenir devant le Seigneur de toute la terre.
Mngeloyo anandiyankha kuti, “Imeneyi ndi mizimu inayi yakumwamba, imene ikuchokera pamaso pa Ambuye wa dziko lonse.
6 Or les chevaux noirs s'en allaient sur toute la terre du septentrion; et les chevaux blancs venaient ensuite; et les gris-pommelé s'en allaient sur la terre du midi;
Galeta la akavalo akuda likupita ku dziko la kumpoto, galeta la akavalo oyera likutsatira, ndipo galeta la akavalo amawanga ofiirira likupita ku dziko la kummwera.”
7 et les autres sortirent, et ils regardèrent pour s'en aller et parcourir toute la terre; et l'ange leur dit: Marchez et parcourez toute la terre. Et ils parcoururent toute la terre.
Pamene akavalo amphamvuwa ankapita, anali ndi changu chofuna kuyendera dziko lapansi. Ndipo iye anati, “Pitani, kayendereni dziko lapansi!”
8 Et il cria, et il me parla, disant: Voilà que ceux qui s'en vont sur la terre du septentrion ont satisfait à Ma colère, en la terre du septentrion.
Pamenepo anandiyitana, “Taona, akavalo amene apita ku dziko la kumpoto apumulitsa Mzimu wanga kumeneko.”
9 Et la parole du Seigneur vint à moi, disant:
Yehova anayankhula nane kuti,
10 Prends les dons des captifs, soit de leurs princes, soit des hommes serviables de la captivité, soit de ceux qui l'honorent; et ce jour-là entre en la maison de Josias, fils de Sophonie, qui est arrivé de Babylone.
“Landira mphatso kuchokera kwa anthu amene abwera ku ukapolo, Helidai, Tobiya ndi Yedaya, amene achokera ku Babuloni. Tsiku lomwelo pita ku nyumba ya Yosiya mwana wa Zefaniya.
11 Et tu prendras l'argent et l'or, et tu en feras des couronnes, et tu les poseras sur la tête de Jésus, fils de Josédec, le grand prêtre.
Tenga siliva ndi golide upange chipewa chaufumu, ndipo uchiyike pamutu pa mkulu wa ansembe, Yoswa mwana wa Yehozadaki.
12 Et tu lui diras: Voici ce que dit le Seigneur tout-puissant: Voilà un homme: Orient est Son Nom, et Il Se lèvera venant de ce qui est sous Lui.
Muwuze kuti zimene akunena Yehova Wamphamvuzonse ndi izi: ‘Taonani, munthu wotchedwa Nthambi ndi ameneyu, ndipo adzaphuka pomwe alipo ndi kumanga Nyumba ya Yehova.
13 Et Il bâtira le temple du Seigneur, et Il recevra la force, et Il siégera, et Il régnera sur Son trône; et le prêtre sera à Sa droite, et un conseil de paix sera entre eux deux.
Ndiye amene adzamange Nyumba ya Yehova, adzalandira ulemerero waufumu ndipo adzalamulira pa mpando wake waufumu. Adzakhalanso wansembe pa mpando wake waufumu. Ndipo padzakhala mtendere.’
14 Et la couronne sera pour ceux qui ont souffert patiemment, et pour ceux de la captivité qui auront été serviables, et pour ceux qui l'ont honorée, afin de rendre des actions de grâces au fils de Sophonie; et les chanter dans le temple du Seigneur.
Chipewa cha ufumucho adzachipereka kwa Helemu, Tobiya, Yedaya, ndi kwa Heni mwana wa Zefaniya, kuti chikhale chikumbutso mʼNyumba ya Yehova.
15 Et ceux qui demeurent au loin viendront et travailleront aussi à réédifier le temple du Seigneur; et vous saurez que le Seigneur tout-puissant M'a envoyé près de vous; et ces choses arriveront si vous êtes dociles à la voix du Seigneur votre Dieu.
Anthu okhala kutali adzabwera kudzathandiza kumanga Nyumba ya Yehova, ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. Zimenezi zidzachitika ngati mudzamvera mwachangu Yehova Mulungu wanu.”

< Zacharie 6 >