< Ruth 3 >
1 Or, comme elle était assise auprès de sa belle-mère, Noémi sa belle-mère lui dit: Fille, ne chercherai-je point pour toi la repos afin que tu sois heureuse?
Tsiku lina Naomi anafunsa mpongozi wake Rute kuti, “Mwana wanga, kodi si kwabwino kuti ndikupezere kokhala kuti zinthu zizikuyendera bwino?
2 Maintenant, Booz, dont tu as fréquenté les filles, ne nous est-il pas connu? Écoute: Il doit vanner cette nuit de l'orge dans son aire.
Bowazi amene adzakazi ake wakhala nawo nthawi yonseyi, si wachibale wathu kodi? Usiku uno akhala akupeta barele ku malo opunthira.
3 Lave-toi donc et te parfume, revêts-toi de ton bel habillement et monte à son aire. Ne te montre pas à l'homme qu'il n'ait fini de manger et de boire.
Samba ndi kudzola mafuta onunkhira, ndipo uvale zovala zako zabwino kwambiri. Kenaka upite ku malo opunthirako tirigu ndi barele koma munthuyo asakakuzindikire kufikira atamaliza kudya ndi kumwa.
4 Lorsqu'il sera couché, et que tu sauras le lieu où il sera couché, tu iras, tu lèveras ce qui couvre ses pieds, tu te coucheras, et lui-même t'apprendra ce que tu auras à faire.
Akamakagona, iwe ukaonetsetse malo amene wagonawo. Kenaka upite ndi kuvundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona. Iyeyo akakuwuza zoti uchite.”
5 Et Ruth répondit: Je ferai tout ce que tu viens de dire.
Rute anayankha kuti, “Ndichita zonse zimene mwanena.”
6 Et elle se rendit à l'aire, et elle fit tout ce que sa belle-mère lui avait recommandé.
Choncho Rute anapita ku malo opunthirawo ndipo anachita monga momwe apongozi ake anamuwuza.
7 Et Booz mangea et il but; son cœur fut réjoui et il alla se coucher au coin d'un tas de blé; elle le suivit en silence et elle leva ce qui couvrait ses pieds.
Atamaliza kudya ndi kumwa, Bowazi anakhala wosangalala, ndipo anakagona pa mbali pa mulu wa barele. Tsono Rute anapita mwa kachetechete, navundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona.
8 Or, à minuit l'homme s'éveilla, et il fut saisi d'étonnement et de trouble en voyant une femme couchée à ses pieds.
Tsono pakati pa usiku Bowazi anadzidzimuka, natembenuka, ndipo anangoona mkazi akugona ku mapazi ake.
9 Et il dit? Qui es-tu? Elle répondit: Je suis Ruth la servante, et tu étendras, ton aile sur ta servante, parce que tu es rédempteur.
Iye anafunsa kuti, “Ndiwe yani?” Ndipo anayankha kuti, “Ndine mdzakazi wanu Rute. Popeza ndinu wachibale amene muyenera kundiwombola, ndiye mundilowe chokolo.”
10 Et Booz reprit: Bénie sois-tu au nom du Seigneur, ma fille, parce que tu as été bonne et miséricordieuse à la fin plus encore qu'au commencement, et que tu n'as recherché les jeunes gens pauvres ou riches.
Ndipo Bowazi anati, “Mwana wanga, Yehova akudalitse popeza kukoma mtima kumene wasonyeza panoku kwaposa koyamba kaja. Iwe sunathamangire anyamata olemera kapena osauka.
11 Maintenant, ma fille, n'aie point de crainte: tout ce que tu demanderas, je te l'accorderai; car toute la tribu de mon peuple sait que tu es une femme forte.
Ndipo tsopano mwana wanga usaope. Ine ndidzakuchitira chilichonse udzapemphe popeza anzanga onse amʼmudzi muno akudziwa kuti ndiwe mkazi wa khalidwe labwino.
12 Il est vrai que je suis ton parent, mais il en est un plus proche que moi.
Ngakhale kuti ndinedi wachibale woyenera kukusamala, koma alipo wachibale weniweni kuposa ine.
13 Demeure ici la nuit et demain: sil veut t'épouser, qu'il t'épouse; mais s'il ne veut t'épouser, je t'épouserai moi, vive le Seigneur. Couche-toi donc, jusqu'à l'aurore.
Gona konkuno usiku uno mpaka mmawa. Tsono ngati iyeyu adzakulowa chokolo, chabwino alowe. Koma ngati safuna kutero, ine ndikulumbira pamaso pa Yehova Wamoyo kuti ndidzakulowa chokolo. Ugone kuno mpaka mmawa.”
14 Elle resta couchée à ses pieds jusqu'au lendemain; puis elle se leva avant que l'on pût se reconnaître de près, et Booz lui dit: Que personne ne sache qu'une femme est venue à mon aire.
Choncho Rute anagona ku mapazi ake mpaka mmawa, koma anadzuka mmamawa kusanayere chifukwa Bowazi anati, “Aliyense asadziwe kuti kopondera barele kunabwera mkazi.”
15 Il ajouta: Soulève le manteau que tu portes; elle le soutint, et il y versa six mesures d'orge; il l'en chargea, et elle rentra dans la ville.
Bowazi anati kwa Rute, “Bwera nacho kuno chofunda wavalacho ndipo uchiyale pansi.” Ndipo atayala, Bowazi anathira makilogalamu makumi awiri a barele ndi kumusenzetsa Rute. Rute anapita nakalowa mu mzinda.
16 Et Ruth alla retrouver sa belle-mère, et celle-ci lui dit: Ma fille! et l'autre, lui raconta tout ce que l'homme avait fait pour elle.
Rute atafika kwa apongozi ake anamufunsa kuti, “Zinayenda bwanji mwana wanga?” Kenaka iye anafotokoza zonse zimene Bowazi anamuchitira.
17 Elle ajouta: Il m'a donné ces dix mesures d'orge, et il m'a dit: Tu ne rentreras pas les mains vides chez ta belle-mère.
Ndipo anati, “Munthuyo anandipatsa makilogalamu makumi awiri awa a barele, nandiwuza kuti usapite kwa apongozi ako wopanda kanthu.”
18 Or, celle-ci dit: Ne bouge pas, fille, jusqu'à ce que tu apprennes que la chose a réussi, car l'homme n'aura pas de repos qu'il ne l'ait terminée aujourd'hui même.
Kenaka Naomi anati, “Mwana wanga, dikira mpaka titaona mmene zinthu zikhalire chifukwa munthuyu salekera pomwepo, mpaka zinthuzi zitakonzeka lero.”