< Psaumes 97 >

1 Pour David, quand son territoire fut établi. Le Seigneur a régné; que la terre tressaille d'allégresse; que la multitude des îles se réjouisse.
Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
2 Les ténèbres et les nuées l'entourent; la justice et le jugement dirigent son trône.
Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 La flamme le précède, et dans son parcours elle brûlera ses ennemis.
Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 Les éclairs ont lui sur le globe de la terre; la terre les a vus et en a tremblé.
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 Les montagnes ont fondu, comme la cire, devant la face du Seigneur; toute la terre a fondu devant sa face.
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 Les cieux ont annoncé sa justice, et tous les peuples ont vu sa gloire.
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 Que tous ceux qui adorent des sculptures, et se glorifient dans leurs idoles, soient confondus! Et vous tous, ses anges, adorez-le!
Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
8 Sion l'a entendu, et elle s'est réjouie; et les filles de Juda ont tressailli d'allégresse à cause de tes jugements, Seigneur.
Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 Car tu es le Seigneur, le Très-Haut, sur toute la terre; tu es digne de louanges infinies, plus que tous les dieux.
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 Vous qui aimez le Seigneur, haïssez le mal; le Seigneur garde les âmes de ses saints, il les délivrera de la main des pécheurs.
Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 La lumière s'est levée pour le juste, et la joie pour ceux qui ont le cœur droit.
Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 Justes, réjouissez-vous dans le Seigneur, et publiez la mémoire de sa sainteté.
Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.

< Psaumes 97 >