< Psaumes 96 >

1 Quand le temple fut rebâti après la captivité, cantique de David. Chantez au Seigneur un cantique nouveau; que toute la terre chante au Seigneur!
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 Chantez au Seigneur; bénissez son nom; publiez avec joie son salut de jour en jour.
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Publiez aux Gentils sa gloire, et ses merveilles à tous les peuples,
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 Car le Seigneur est grand et digne de louanges infinies; il est plus terrible que tous les dieux.
Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 Car tous les dieux des Gentils sont des démons; mais le Seigneur a créé les cieux.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 Louanges et beauté sont en sa présence; la sainteté et la majesté sont en son sanctuaire.
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 Tribus des Gentils, rendez au Seigneur, rendez à Dieu gloire et honneur.
Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 Rendez gloire au Seigneur et à son nom; prenez des victimes et entrez dans ses parvis.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 Adorez le Seigneur en son temple saint, et que devant sa face tremble toute la terre.
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 Dites aux Gentils: Le Seigneur règne, car il a affermi le globe de la terre, et il ne sera plus ébranlé; il jugera les peuples avec droiture.
Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Que les cieux se réjouissent et que la terre tressaille d'allégresse; que la mer en sa plénitude soit émue.
Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 Les champs et tout ce qu'ils renferment se réjouiront; alors tressailliront les arbres de la forêt
minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 Devant la face du Seigneur; car il vient, car il vient juger la terre. Il jugera le monde selon sa justice, et les peuples selon sa vérité.
idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

< Psaumes 96 >