< Psaumes 87 >
1 Psaume et cantique des fils de Koré. Les fondements de Sion sont sur les montagnes saintes.
Salimo la Ana a Kora. Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
2 Le Seigneur aime ses portes plus que toutes les tentes de Jacob.
Yehova amakonda zipata za Ziyoni kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
3 On a dit de toi des choses glorieuses, ô cité de Dieu!
Za ulemerero wako zimakambidwa, Iwe mzinda wa Mulungu: (Sela)
4 Je rappellerai Raab et Babylone à ceux qui me connaissent. Et voilà que les étrangers et Tyr, et le peuple des Éthiopiens s'y sont réunis.
“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni pakati pa iwo amene amandidziwa. Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi, ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’”
5 Un homme dira: Ma mère est Sion; et cet homme y est né, et le Très-Haut lui-même en a été le fondateur.
Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti, “Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye, ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
6 Le Seigneur racontera cela dans l'écrit des peuples et des princes qui sont nés dans Sion.
Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina: “Uyu anabadwira mʼZiyoni.” (Sela)
7 Pour tous, habiter en toi, c'est habiter dans la joie.
Oyimba ndi ovina omwe adzati, “Akasupe anga onse ali mwa iwe.”