< Psaumes 82 >
1 Psaume d'Asaph. Dieu s'est tenu debout dans l'assemblée des dieux, et Dieu jugera au milieu.
Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
2 Jusques à quand jugerez-vous selon l'iniquité, et aurez-vous égard à la face des pécheurs?
“Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
3 Jugez l'orphelin et le pauvre; justifiez l'humble et l'indigent.
Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4 Délivrez l'indigent, et retirez le pauvre de la main du pécheur.
Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
5 Ils ne savent pas, ils n'ont point compris; ils cheminent dans les ténèbres; tous les fondements de la terre seront ébranlés.
“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6 Et moi j'ai dit: vous êtes des dieux, et tous fils du Très-Haut.
“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7 Cependant vous mourrez comme des hommes et vous tomberez comme l'un des princes.
Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
8 Lève-toi, ô Dieu, juge la terre; car toutes les nations seront ton héritage.
Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.