< Psaumes 77 >

1 Jusqu'à la Fin. Psaume d'Asaph, sur Idithun. J'ai crié au Seigneur de ma voix; et ma voix est allée au Seigneur, et il a fait attention à moi.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
2 Au jour de mon affliction, j'ai cherché Dieu; la nuit, j'ai étendu vers lui les mains, et je n'ai pas été déçu. Mon âme ne voulait pas être consolée.
Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
3 Je me suis souvenu de Dieu, et j'ai été réjoui; j'ai réfléchi comme un enfant, et mon esprit a défailli.
Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
4 Tous mes ennemis surprenaient à l'improviste mes gardes; j'ai été troublé, et je n'ai point parlé.
Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
5 J'ai considéré les jours antiques, et je me suis souvenu des années éternelles.
Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
6 J'ai médité, et la nuit j'ai réfléchi en mon cœur, et je me suis creusé l'esprit, disant:
Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
7 Est-ce que le Seigneur me repoussera toujours? est-ce qu'il ne se complaira plus en moi?
“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
8 Est-ce que, jusqu'à la fin, il privera de sa miséricorde les générations des générations?
Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
9 Dieu oubliera-t-il de s'apitoyer? Confondrait-il sa miséricorde avec sa colère?
Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
10 Et j'ai dit: Maintenant j'ai commencé; ceci est le changement de la droite du Très-Haut.
Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
11 Je me suis souvenu des œuvres du Seigneur, et je me souviendrai de tes merveilles dès le commencement.
Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
12 Et je méditerai sur toutes tes œuvres, et je réfléchirai sur tes conseils.
Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
13 O Dieu, ta voie est dans la sainteté; quel Dieu est grand comme notre Dieu?
Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
14 Tu es le Dieu qui fait tes merveilles; tu as fait connaître aux peuples ta puissance.
Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
15 Par ton bras, tu as délivré ton peuple, les fils de Jacob et de Joseph.
Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
16 Les eaux t'ont vu, mon Dieu, les eaux t'ont vu; et elles ont eu peur, et les abîmes ont été troublés.
Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
17 Le fracas des eaux a longuement retenti; les nuées ont fait entendre des voix, car tes flèches les ont traversées.
Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
18 La voix de ton tonnerre a retenti dans la voûte du ciel; tes éclairs ont brillé sur le monde; la terre a frémi et tremblé.
Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
19 Ta voie est au fond de la mer; et tes sentiers sont recouverts par des amas d'eau, et l'on ne reconnaîtra pas tes traces.
Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
20 Tu as conduit ton peuple comme un troupeau par les mains d'Aaron et de Moïse.
Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.

< Psaumes 77 >