< Psaumes 76 >

1 Jusqu'à la Fin. Jusqu'à la Fin avec les hymnes, psaume d'Asaph, chant concernant les Assyriens. Dieu est connu en Judée; son nom est grand en Israël.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
2 Et son lieu est dans la paix, et sa demeure est dans Sion.
Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
3 C'est là qu'il a brisé la force des arcs, et les armures, et le glaive, et la guerre.
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
4 Tu éclaires merveilleusement du haut des montagnes éternelles.
Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
5 Tous les insensés ont été troublés en leur cœur. Ils ont dormi leur sommeil, et tous les favoris de la richesse n'ont rien trouvé dans leurs mains.
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
6 A tes approches, Dieu de Jacob, les cavaliers se sont endormis sur leurs chevaux.
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
7 Tu es redoutable, et qui donc résisterait à ta colère?
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
8 Du haut du ciel tu as fait entendre ton jugement; la terre a eu peur, et s'est tenue en repos,
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
9 Lorsque Dieu s'est levé pour juger et pour sauver les doux en leur cœur.
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
10 La pensée de l'homme te rendra grâces, et le mémorial de cette pensée te fêtera.
Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
11 Faites des vœux à Dieu notre Seigneur, et accomplissez-les; tous ceux qui se rassemblent autour de lui feront des offrandes au Dieu terrible,
Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
12 A celui qui ôte l'esprit aux princes et qui est terrible aux rois de la terre.
Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.

< Psaumes 76 >