< Psaumes 73 >

1 Psaume d'Asaph. Que Dieu est bon pour Israël, pour ceux qui sont droits en leur cœur!
Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
2 Peu s'en est fallu que mes pieds n'aient chancelé; peu s'en est fallu que mes pieds n'aient glissé.
Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
3 Car à voir la paix des pécheurs, je les avais enviés.
Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
4 En effets à leur mort ils ne font point paraître qu'ils la refusent, et ils ont de la fermeté en leurs châtiments.
Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
5 Ils n'ont point les peines des autres hommes, et comme les autres hommes ils ne seront point flagellés.
Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
6 A cause de cela l'orgueil les possède; ils se sont revêtus de leur injustice et de leur impiété.
Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
7 Leur injustice sortira de leur richesse comme de sa source; ils se sont adonnés aux caprices de leur cœur.
Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
8 Ils ont pensé et parlé méchamment; ils ont parlé du Très-Haut avec injustice.
Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
9 Ils ont fait usage de leur bouche contre le ciel, et leur langue a parcouru la terre.
Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
10 A cause de cela mon peuple y retournera, et une grande plénitude de jours sera trouvée en eux.
Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
11 Ils ont dit: Que sait Dieu? et comment y a-t-il quelque science dans le Très -Haut?
Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
12 Voilà les pécheurs qui prospèrent toujours; ils possèdent les richesses.
Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
13 Et moi-même j'ai dit: J'ai donc vainement rendu juste mon cœur, et levé mes mains parmi les innocents!
Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
14 J'ai été châtié tout le jour, et réprimandé tous les matins.
Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
15 Si j'avais parlé ainsi, voilà que j'eusse rompu mon alliance avec vos enfants.
Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
16 Et J'ai entrepris de comprendre ces choses; mais ce travail reste inconnu devant moi,
Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
17 Tant que je n'aurai pas pénétré dans le sanctuaire de Dieu; car c'est ainsi que je comprendrai les choses de la fin.
kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
18 Or donc, Seigneur, tu as rendu jugement contre eux à cause de leurs fourberies; et tandis qu'ils s'élevaient, tu les as renversés.
Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
19 Comment sont-ils tombés dans la désolation? Ils ont défailli soudain; ils ont péri à cause de leur iniquité.
Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
20 Comme le songe d'un homme qui s'éveille, Seigneur, dans ta cité tu mets à néant leur image.
Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
21 C'est pourquoi mon cœur s'est réjoui, et mes reins se sont reposés.
Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
22 Parce que moi aussi j'avais été mis à néant, et j'en ignorais la cause;
ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
23 Devant toi, j'étais devenu comme une brute, et je restai sans cesse avec toi.
Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
24 Mais tu m'as pris par la main droite, tu m'as conduit selon ta volonté; tu m'as accueilli avec honneur.
Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
25 Or, qu'ai-je au ciel? Et après toi, qu'ai-je désiré sur la terre?
Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
26 Ma chair et mon cœur ont défailli, ô Dieu de mon cœur, et Dieu est mon partage pour toujours.
Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
27 Car ceux qui se sont éloignés de toi périront, et tu as exterminé tous ceux qui se prostituaient loin de toi.
Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
28 Pour moi, il est bon que je m'attache à Dieu, que je place en Dieu mon espérance, que je chante ses louanges aux portes de la fille de Sion.
Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.

< Psaumes 73 >