< Psaumes 71 >

1 De David, un psaume chanté par les fils de Jonadab et les chefs lorsqu'ils étaient prisonniers. Seigneur, j'ai espéré en toi; que je ne sois pas confondu à jamais.
Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
2 Dans ta justice défends-moi, et délivre-moi; incline vers moi ton oreille, et sauve-moi.
Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
3 Sois pour moi un Dieu protecteur et une place fortifiée, afin de me sauver; car tu es mon appui et mon refuge.
Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
4 Mon Dieu, tire-moi de la main du pécheur, de celle du pervers et du méchant.
Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
5 Car tu es mon attente, Seigneur; Seigneur, tu es mon espérance dès ma jeunesse.
Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
6 A peine conçu, j'ai été confirmé en toi; dès le sein de ma mère, tu es mon abri; mes chants ne cessent de s'adresser à toi.
Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
7 J'ai été comme un prodige pour un grand nombre; et toi, tu es ma force et mon appui.
Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
8 Que ma bouche soit pleine de louanges, afin que je chante tout le jour ta gloire et ta grandeur.
Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
9 Ne me fais point tomber au temps de la vieillesse; quand ma force sera défaillante, ne m'abandonne pas.
Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
10 Car mes ennemis ont parlé contre moi; ceux qui épient mon âme ont tenu conseil ensemble,
Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
11 Disant: Dieu l'a délaissé, poursuivez-le, saisissez-le; car nul n'est là pour le défendre.
Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
12 Dieu, ne t'éloigne point de moi; mon Dieu, viens à mon aide!
Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
13 Qu'ils soient confondus et détruits, les calomniateurs de mon âme; qu'ils soient revêtus de honte et d'humiliation, ceux qui me veulent du mal.
Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
14 Pour moi, j'espérerai toujours; je te louerai de plus en plus.
Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
15 Ma bouche proclamera tout le jour ta justice et ton salut; car je ne connais pas les œuvres intellectuelles.
Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
16 Mais j'entrerai dans la contemplation de la puissance de Dieu; Seigneur, je me souviendrai seulement de ta justice.
Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
17 Tu m'as instruit, Seigneur, dès ma jeunesse, et jusqu'ici j'ai annoncé tes merveilles.
Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
18 Et je continuerai jusqu'à l'extrême vieillesse; ô Dieu, ne m'abandonne pas avant que j'aie annoncé, à toute la génération future, ton bras et ta puissance,
Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
19 Et ta justice, ô mon Dieu, jusqu'au plus haut des cieux, et les grandes choses que tu as faites. O Dieu, qui donc est semblable à toi?
Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
20 Autant de fois tu m'as fait voir de nombreuses et cruelles afflictions, autant de fois tu es revenu à moi pour me vivifier; et tu m'as ramené des abîmes de la terre.
Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
21 Tu as multiplié sur moi ta libéralité, et tu es revenu à moi, et tu m'as consolé, et tu m'as ramené des abîmes de la terre.
Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
22 Et moi, sur mes instruments de musique, je confesserai, ô mon Dieu, ta vérité; je te chanterai des psaumes sur la cithare, ô Saint d'Israël!
Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
23 Mes lèvres se réjouiront quand je chanterai pour toi, et aussi mon âme que tu as affranchie.
Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
24 Ma langue, tout le jour, racontera ta justice, lorsque ceux qui me veulent du mal auront été humiliés et confondus.
Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.

< Psaumes 71 >