< Psaumes 67 >

1 Jusqu'à la Fin, psaume d'un des hymnes de David, Dieu, aie pitié de nous et bénis-nous; fais luire sur nous ton visage,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
2 Pour qu'en cette terre nous connaissions ta voie, et que le salut soit parmi toutes les nations.
Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
3 Que les peuples te rendent grâces, ô Dieu! que tous les peuples te rendent grâces!
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
4 Que les nations se réjouissent et tressaillent, parce que tu jugeras les peuples en ta droiture, et que tu guideras les nations sur la terre!
Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
5 Que les peuples te rendent grâces, ô Dieu! que tous les peuples te rendent grâces!
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
6 La terre a donné son fruit; que Dieu, que notre Dieu nous bénisse!
Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
7 Que Dieu nous bénisse, et que tous les confins de la terre le craignent!
Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.

< Psaumes 67 >