< Psaumes 65 >

1 Jusqu'à la Fin. Hymne de David, inspiré des paroles de Jérémie et Ezéchiel à l'époque de la déportation, et quand ils étaient sur le point de sortir. O Dieu, il convient en Sion de te chanter des hymnes; et des vœux te seront rendus.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo. Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni; kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
2 Exauce ma prière; toute chair ira à toi.
Inu amene mumamva pemphero, kwa inu anthu onse adzafika.
3 Les paroles des méchants ont prévalu contre nous; mais tu nous pardonneras nos impiétés.
Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo, Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
4 Heureux celui que tu auras élu et adopté; il habitera en tes parvis. Nous nous rassasierons des biens de ta demeure. Ton temple est saint; il est admirable en justice.
Odala iwo amene inu muwasankha ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu! Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu, za mʼNyumba yanu yoyera.
5 Exauce-nous, ô Dieu notre Sauveur, espérance de toute la terre et de ceux qui sont au loin sur la mer.
Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo, Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
6 Par ta force tu as formé les monts; tu es revêtu de puissance.
amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu, mutadziveka nokha ndi mphamvu.
7 Tu ébranles l'abîme de la mer, et ses flots retentissent; et les nations seront troublées.
Amene munakhalitsa bata nyanja kukokoma kwa mafunde ake, ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
8 Et ceux qui demeurent aux confins de la terre seront saisis de crainte, à cause de tes signes; tu répandras la joie de l'Orient à l'Occident.
Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu; kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera. Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
9 Tu as visité la terre, et tu l'as enivrée; tu as multiplié tes dons pour l'enrichir. Le fleuve de Dieu a été rempli d'eau; tu as préparé leur nourriture: voilà comment est fertilisée la terre.
Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira; Inuyo mumalilemeretsa kwambiri. Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi kuti upereke tirigu kwa anthu, pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10 Abreuve ses sillons, multiplie ses fruits; la récolte qui germe se réjouira de ses rosées.
Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake, mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11 Tu béniras le cercle des mois qui est la couronne de ta bonté, et tes champs seront remplis d'abondance.
Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka, ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12 Les montagnes du désert seront engraissées, et les collines seront revêtues d'allégresse.
Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira; mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13 Les béliers du troupeau sont couverts de toison; les vallées regorgeront de froment; elles crieront, et chanteront un hymne au Seigneur.
Madambo akutidwa ndi zoweta ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu; izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.

< Psaumes 65 >