< Psaumes 63 >
1 Psaume de David, quand il était dans l'Idumée. Dieu, ô mon Dieu, je veille pour toi dès l'aurore; mon âme a soif de toi; avec quelle ardeur ma chair te désire!
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 Sur une terre déserte, sans chemin et sans eau, je me tiens devant toi, comme dans ton sanctuaire, pour contempler ta puissance et ta gloire.
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 Ta miséricorde est préférable à toutes les vies, aussi mes lèvres te loueront-elles.
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 Je te bénirai tant que durera ma vie; j'élèverai les mains en ton nom.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 Que mon âme soit remplie de moelle et de graisse, et que mes lèvres joyeuses chantent ton nom.
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 Je me suis souvenu de toi sur ma couche; dès l'aurore, je méditais sur toi.
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 Car tu as été mon champion, et à l'ombre de tes ailes je tressaillirai de joie.
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 Mon âme s'est attachée à te suivre, et ta droite m'a soutenu.
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 Vainement ils ont cherché mon âme; ils seront précipités dans les entrailles de la terre.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 Ils seront livrés à la violence du glaive; ils seront la proie des renards.
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 Cependant le roi se réjouira en Dieu; quiconque jure en lui sera loué, parce qu'il aura fermé la bouche de ceux qui proféraient l'iniquité.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.