< Psaumes 59 >
1 Jusqu'à la Fin, avec cette inscription de David: Ne détruis pas; quand Saül envoya et fit garder sa maison pour le mettre à mort. O Dieu, délivre-moi de mes ennemis; délivre-moi de ceux qui s'élèvent contre moi.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
2 Délivre-moi des ouvriers d'iniquité, et sauve-moi des hommes de sang.
Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
3 Car voilà qu'ils ont fait la chasse à mon âme; des hommes puissants se sont jetés sur moi.
Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
4 Ce n'est ni mon iniquité ni mon péché, Seigneur, qui en sont la cause: exempt d'iniquité, j'ai couru droit devant moi.
Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
5 Réveille-toi, viens à mon aide, et vois, Seigneur, Dieu des vertus. Dieu d'Israël; sois attentif à visiter les nations; n'aie aucune pitié pour ceux qui commettent l'iniquité.
Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
6 Ils viendront sur le soir, et ils seront affamés comme des chiens, et ils courront autour de la ville.
Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
7 Voilà qu'ils vociféreront, et ils auront une épée sur les lèvres: Qui nous entend? s'écrieront-ils.
Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
8 Et toi, Seigneur, tu riras d'eux; tu réduiras toutes les nations à néant.
Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
9 Je garderai ma force en toi; car ô mon Dieu, tu es mon défenseur.
Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
10 Quant à mon Dieu, sa miséricorde me préviendra.
Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
11 Dieu me montrera sa vengeance sur mes ennemis. Ne les fais pas mourir, de peur que ton peuple n'en perde la mémoire. Disperse-les en ta puissance, et renverse-les. Dieu mon protecteur.
Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
12 Châtie le péché de leur bouche, les paroles de leurs lèvres; qu'ils soient punis dans leur orgueil; et l'on s'entretiendra de leurs malédictions, de leurs mensonges.
Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
13 Détruis-les, détruis-les en ta colère; et ils ne subsisteront plus; et l'on saura que le Dieu de Jacob règne jusqu'aux confins de la terre.
muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
14 Ils reviendront sur le soir; ils seront affamés comme des chiens, et ils courront autour de la ville.
Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
15 Ils se disperseront pour manger; et s'ils ne sont point rassasiés, ils murmureront.
Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
16 Pour moi, je chanterai ta puissance, et, dès l'aurore, je me réjouirai de ta miséricorde; car tu es mon défenseur et mon refuge au jour de mon affliction.
Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
17 Je te chanterai mes psaumes, ô mon Sauveur, ô mon Dieu; tu es mon défenseur, mon Dieu et ma miséricorde.
Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.