< Psaumes 57 >

1 Jusqu'à la Fin, avec cette inscription de David: Ne détruis pas; lorsqu'il se réfugia dans la caverne pour se soustraire aux recherches de Saül. Aie pitié de moi, ô mon Dieu, aie pitié de moi, car mon âme s'est confiée en toi; j'espérerai à l'ombre de tes ailes, jusqu'à ce que l'iniquité soit passée.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
2 Je crierai vers le Seigneur très-haut, vers Dieu mon bienfaiteur.
Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
3 Il a envoyé son secours du ciel, et il m'a sauvé; il a livré aux outrages ceux qui me foulaient aux pieds; Dieu m'a envoyé sa miséricorde et sa vérité.
Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
4 Il a tiré mon âme du milieu des lionceaux. J'ai dormi au milieu du trouble. Les fils des hommes ont leurs dents pour armes et pour traits, et leur langue est un glaive aiguisé.
Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
5 Dieu, sois exalté au-dessus des cieux, et que ta gloire soit sur toute la terre.
Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
6 Ils avaient préparé des pièges sur mon passage, et ils avaient fait fléchir mon âme; ils avaient creusé devant mes pas une fosse, et ils y sont tombés.
Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
7 Mon cœur est prêt, ô mon Dieu, mon cœur est prêt; je chanterai, je chanterai des psaumes.
Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
8 Réveille-toi, ô ma gloire; réveillez-vous, ma harpe et ma cithare; je m'éveillerai dès l'aurore.
Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
9 Seigneur, je te confesserai parmi les peuples; je te chanterai parmi les nations.
Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
10 Car ta miséricorde s'élève jusque au-dessus des cieux, et ta vérité jusqu'aux nues.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
11 Dieu, sois exalté au-dessus des cieux, et que ta gloire soit sur toute la terre!
Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.

< Psaumes 57 >