< Psaumes 32 >

1 Un psaume de méditation, de David. Heureux ceux à qui leurs péchés ont été remis, et dont les fautes ont été couvertes.
Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
2 Heureux l'homme à qui le Seigneur n'impute point de péché, et qui n'a pas de fraude sur les lèvres.
Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
3 Parce que j'ai gardé le silence, mes os ont vieilli, quand je criais tout le jour.
Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
4 Jour et nuit ta main s'était appesantie sur moi; je me retournais dans ma détresse, tandis qu'une épine s'enfonçait en moi. Interlude.
Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
5 Je t'ai fait connaître mon péché; je n'ai point caché mon iniquité. J'ai dit: Je confesserai à Dieu mon iniquité contre moi; et tu m'as pardonné l'impiété de mon péché. Interlude.
Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
6 A cause de cela chaque saint te fera sa prière au moment opportun; les grandes eaux même d'un déluge n'approcheront point de lui.
Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
7 Tu es mon refuge dans la tribulation qui m'a environné; à toi, ô ma joie, délivre-moi de ceux qui m'ont investi. Interlude.
Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
8 Je te donnerai l'intelligence et je t'affermirai dans la voie où tu dois marcher; j'aurai toujours les yeux fixés sur toi.
Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
9 Ne soyez pas comme le cheval et le mulet, à qui manque l'intelligence: serre leur bouche avec la bride et le frein, pour qu'ils ne s'approchent point de toi.
Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
10 Les flagellations réservées aux pécheurs sont nombreuses; tandis que la miséricorde du Seigneur entourera celui qui espère en lui.
Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
11 Ô justes, livrez-vous dans le Seigneur à la joie et à tous ses transports; et glorifiez-vous en lui, vous tous dont le cœur est droit.
Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!

< Psaumes 32 >