< Psaumes 31 >
1 Jusqu'à la Fin. Psaume de David, à l'occasion d'une grande terreur. Seigneur, j'ai espéré en toi; que je ne sois point confondu éternellement. Délivre-moi en ta justice, et sauve-moi.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo; musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi; mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
2 Penche vers moi ton oreille; hâte-toi de me sauver; sois-moi un Dieu protecteur, et comme une maison de refuge, afin que je sois sauvé.
Tcherani khutu lanu kwa ine, bwerani msanga kudzandilanditsa; mukhale thanthwe langa lothawirapo, linga lolimba kundipulumutsa ine.
3 Car tu es ma force et mon refuge; et pour l'amour de ton nom tu me guideras et me nourriras.
Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa, chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
4 Tu me tireras de ce piège qu'ils avaient caché pour moi; car tu es mon protecteur.
Ndimasuleni mu msampha umene anditchera pakuti ndinu pothawirapo panga.
5 Je remets mon âme en tes mains; tu m'as racheté, Seigneur, Dieu de vérité.
Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga; womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.
6 Tu hais ceux qui s'attachent follement aux choses vaines; pour moi, j'ai placé mon espérance dans le Seigneur.
Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe; ine ndimadalira Yehova.
7 Je trouverai mon bonheur et ma joie en ta miséricorde; car tu as considéré mon humiliation, tu as sauvé mon âme de sa détresse.
Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu popeza Inu munaona masautso anga ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
8 Tu ne m'as pas enfermé dans les mains de mes ennemis; tu as donné de l'espace à mes pieds.
Inu simunandipereke kwa mdani koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.
9 Aie pitié de moi, Seigneur, parce que je suis affligé; mon œil est troublé par la tristesse, et mon âme, et mes entrailles.
Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto; maso anga akulefuka ndi chisoni, mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
10 Ma vie s'est éteinte dans la douleur, et mes années dans les sanglots; ma force a été brisée par la misère, et mes os ébranlés.
Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula; mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso, ndipo mafupa anga akulefuka.
11 Je suis devenu un signe d'outrage pour tous mes ennemis et surtout pour mes voisins; je suis devenu l'effroi de mes proches; ceux qui m'ont vu se sont enfuis au dehors.
Chifukwa cha adani anga onse, ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga; ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga. Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
12 J'ai été mis en oubli dans les cœurs comme un mort; on m'a traité comme un vase brisé.
Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira; ndakhala ngati mʼphika wosweka.
13 J'ai entendu le blâme de plusieurs qui demeurent autour de moi; pendant qu'ils se réunissaient contre moi, ils ont tenu conseil pour m'ôter la vie.
Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri; zoopsa zandizungulira mbali zonse; iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane, kuti atenge moyo wanga.
14 Mais moi, Seigneur, j'ai mis en toi mon espérance, et j'ai dit: tu es mon Dieu.
Koma ndikudalira Inu Yehova; ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
15 Mon sort est entre tes mains; arrache-moi de la main de mes ennemis et de ceux qui me persécutent.
Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
16 Montre à ton serviteur la lumière de ton visage; sauve-moi par ta miséricorde.
Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu; pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
17 Seigneur, que je ne sois point confondu, car je t'ai invoqué; que les impies rougissent et soient précipités en enfer. (Sheol )
Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol )
18 Que les lèvres trompeuses deviennent muettes; car elles profèrent l'iniquité contre le juste avec orgueil et mépris.
Milomo yawo yabodzayo ikhale chete, pakuti chifukwa cha kunyada ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.
19 Combien est grande, Seigneur, l'abondance de douceur que tu as réservée à ceux qui te craignent! Tu l'as rendue parfaite pour ceux qui espèrent en toi, devant les fils des hommes.
Ndi waukulu ubwino wanu umene mwawasungira amene amakuopani, umene mumapereka anthu akuona kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
20 Ceux-là tu les cacheras dans le secret de ta face pour les préserver du trouble des hommes; tu les mettras en ton tabernacle à l'abri de la contradiction des langues.
Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa, kuwateteza ku ziwembu za anthu; mʼmalo anu okhalamo mumawateteza kwa anthu owatsutsa.
21 Béni soit le Seigneur, parce qu'il m'a merveilleusement manifesté sa miséricorde comme en une ville fortifiée.
Matamando akhale kwa Yehova, pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
22 Et moi j'ai dit dans le transport de mon âme: J'ai été rejeté loin de tes yeux; c'est pourquoi. Seigneur, lorsque j'ai crié vers toi, tu as exaucé la voix de ma prière.
Ndili mʼnkhawa zanga ndinati, “Ine ndachotsedwa pamaso panu!” Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.
23 Aimez le Seigneur, vous tous qui êtes ses saints; car le Seigneur cherche la vérité, et il rétribuera abondamment les superbes.
Kondani Yehova oyera mtima ake onse! Yehova amasunga wokhulupirika koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
24 Soyez hommes; et que votre cœur se fortifie, vous tous qui espérez en Dieu.
Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima, inu nonse amene mumayembekezera Yehova.