< Psaumes 29 >

1 Un psaume de David, à l'occasion de l'assemblée solennelle du Tabernacle. Apportez au Seigneur, enfants de Dieu, apportez au Seigneur les petits des béliers.
Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
2 Rendez au Seigneur gloire et honneur; glorifiez le nom du Seigneur; adorez le Seigneur en son saint parvis.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
3 La voix du Seigneur est sur les eaux; le Dieu de gloire a tonné; le Seigneur est sur les grandes eaux.
Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
4 La voix du Seigneur est puissante; la voix du Seigneur est pleine de magnificence.
Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
5 La voix du Seigneur brise les cèdres; le Seigneur va broyer les cèdres du Liban.
Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
6 Il les brisera comme un jeune taureau du Liban, comme le faon chéri de la licorne.
Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
7 C'est la voix du Seigneur qui divise la flamme et le feu.
Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
8 C'est la voix du Seigneur qui fait trembler le désert; le Seigneur ébranlera le désert de Cadès.
Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
9 C'est la voix du Seigneur qui a préparé la naissance des cerfs; elle découvrira les forêts, et dans le temple du Seigneur chacun dira sa gloire.
Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
10 Le Seigneur répandra sur la terre un déluge; le Seigneur est roi, et il siégera éternellement.
Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
11 Le Seigneur fortifiera son peuple; le Seigneur bénira son peuple en lui donnant la paix.
Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

< Psaumes 29 >