< Psaumes 145 >

1 Louange, de David. Je t'exalterai, ô mon Dieu, ô mon Roi, et je bénirai ton nom dans les siècles, et dans les siècles des siècles.
Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Chaque jour je te bénirai et je louerai ton nom dans les siècles, et dans les siècles des siècles.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 Le Seigneur est grand et digne de louanges infinies; à sa grandeur il n'est point de limite.
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 Les générations des générations loueront tes œuvres; elles proclameront ta puissance.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 Elles diront la majesté de ta sainteté, et raconteront tes merveilles.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 Elles diront la force de tes épouvantements; elles raconteront ta grandeur.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 Elles rappelleront avec effusion le souvenir de ton inépuisable bonté, et se réjouiront de ta justice.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 Le Seigneur est compatissant et miséricordieux; il est longanime et plein de miséricorde.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 Le Seigneur est doux pour ceux qui l'attendent, et ses miséricordes sont encore au-dessus de toutes ses œuvres.
Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Seigneur, que toutes tes œuvres te louent, et que tes saints te bénissent.
Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
11 Qu'ils disent la gloire de ton royaume; qu'ils parlent de ta domination;
Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 Pour faire connaître aux fils des hommes ta puissance et la majesté glorieuse de ta royauté.
kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Ton royaume est le royaume de tous les siècles, et ta domination va de génération en génération; le Seigneur est fidèle en ses paroles; et saint en toutes ses œuvres.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Le Seigneur affermit ceux qui tombent; il relève ceux qui ont été brisés.
Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Les yeux de tous espèrent en toi, et tu leur donne la nourriture en temps opportun.
Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Tu ouvres les mains, et tu remplis de bénédiction tout être animé.
Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 Le Seigneur est juste en toutes ses voies, et saint en toutes ses œuvres.
Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Le Seigneur est proche de ceux qui l'invoquent, de tous ceux qui l'invoquent en vérité.
Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Il fera la volonté de ceux qui le craignent, et il exaucera leurs prières, et il les sauvera.
Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Le Seigneur garde tous ceux qui l'aiment, et il exterminera tous les pécheurs.
Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 Que ma bouche dise les louanges du Seigneur, et que toute chair bénisse son saint nom dans les siècles, et dans les siècles des siècles.
Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.

< Psaumes 145 >