< Psaumes 135 >
1 Alléluiah! Louez le Seigneur, ô vous qui êtes ses serviteurs; louez le Seigneur!
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 Vous qui vous tenez en sa maison, dans les parvis de la maison de notre Dieu,
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Louez le Seigneur, parce que le Seigneur est bon; chantez des psaumes à son nom, parce que son nom est beau.
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 Car le Seigneur a choisi Jacob pour être à lui Jacob, et Israël pour être sa possession.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 Et moi j'ai reconnu que le Seigneur est grand, que notre Dieu est au- dessus de tous les dieux.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 Tout ce que le Seigneur a voulu, il l'a fait; dans le ciel et sur la terre, et dans la mer, et dans tous les abîmes.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 Il amène les nuées des extrémités de la terre; il change les éclairs en pluie. C'est lui qui tire les vents de ses trésors.
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 C'est lui qui a frappé les premiers-nés d'Egypte, depuis l'homme jusqu'aux troupeaux;
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 Lui qui a envoyé ses signes et ses prodiges au milieu de toi, Egypte, devant le Pharaon et tous ses serviteurs;
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 Lui qui a frappé maintes nations et tué des rois puissants:
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Séhon, roi des Amorrhéens et Og, roi de Basan, et tous les rois chananéens;
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 Et qui a donné leur héritage en héritage à Israël, son peuple.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 Seigneur, ton nom est éternel, et ta mémoire passe de génération en génération.
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 Car le Seigneur jugera son peuple, et il écoutera les prières de ses serviteurs.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 Les idoles des Gentils sont argent et or, œuvres des mains des hommes.
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 Elles ont une bouche, et ne parleront pas; elles ont des yeux, et ne verront pas.
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 Elles ont des oreilles, et n'entendront pas [des narines, et ne sentent pas, des mains et ne touchent pas, des pieds et ne marchent pas, et il n'y a pas de voix dans leur gosier]; et il n'est point de souffle en leur bouche.
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Que ceux qui les font leur deviennent semblables, et tous ceux qui croient en elles.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 Maison d'Israël, bénis le Seigneur; maison d'Aaron, bénis le Seigneur.
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 Maison de Lévi, bénis le Seigneur; vous qui craignez le Seigneur, bénissez le Seigneur.
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Béni soit le Seigneur en Sion, lui qui habite Jérusalem!
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.