< Psaumes 128 >

1 En Jérusalem. Heureux tous ceux qui craignent le Seigneur et qui cheminent en ses voies.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
2 Tu mangeras le fruit des labeurs de tes mains; tu es heureux, et tu prospéreras.
Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
3 Ta femme sera comme une vigne féconde dans l'enceinte de ta maison; et tes enfants autour de ta table seront comme de jeunes plants d'olivier.
Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
4 Voilà comme sera béni l'homme qui craint le Seigneur.
Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
5 Que le Seigneur du haut de Sion te bénisse; et que tu voies les biens de Jérusalem, tous les jours de ta vie.
Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
6 Et que tu voies les fils de tes fils: paix sur Israël!
ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.

< Psaumes 128 >