< Psaumes 125 >
1 Cantique des degrés. Ceux qui ont foi dans le Seigneur sont comme la montagne de Sion. Il ne sera point ébranlé dans les siècles des siècles, celui qui habite en Jérusalem.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni, limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.
2 Des montagnes sont alentour, et le Seigneur à l'entour de son peuple, maintenant et dans les siècles des siècles.
Monga mapiri azungulira Yerusalemu, momwemonso Yehova azungulira anthu ake kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 Le Seigneur ne permettra pas que la verge des pécheurs soit toujours sur l'héritage des justes, de peur que les justes n'étendent leurs mains à l'iniquité.
Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama, kuti anthu olungamawo angachite nawonso zoyipa.
4 Seigneur: bénis les bons et ceux qui ont le cœur droit.
Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino, amene ndi olungama mtima
5 Ceux qui vont dans les sentiers détournés, le Seigneur les conduira parmi les ouvriers d'iniquité: paix sur Israël!
Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa. Mtendere ukhale pa Israeli.