< Psaumes 122 >

1 Cantique des degrés. Je me suis réjoui quand ils m'ont dit: Entrons dans la maison du Seigneur.
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
2 Nos pieds étaient fermes jadis en tes parvis, ô Jérusalem.
Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
3 Jérusalem est bâtie comme une ville dont toutes les parties sont parfaitement unies.
Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
4 Car c'est là que montaient les tribus, les tribus du Seigneur, selon l'ordre donné à Israël, pour rendre gloire au nom du Seigneur.
Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
5 Là étaient établis des trônes pour le jugement, des trônes pour la maison de David.
Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
6 Priez pour la paix de Jérusalem, et la prospérité de ceux qui t'aiment, ô cité sainte!
Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
7 Que la paix règne dans ta force, et l'abondance dans tes tours.
Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
8 J'ai désiré pour toi la paix, à cause de mes frères et de mes proches.
Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
9 J'ai cherché ce qui t'est bon, à cause de la maison du Seigneur notre Dieu.
Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.

< Psaumes 122 >