< Psaumes 121 >

1 Cantique des degrés. J'ai levé les yeux vers les montagnes, d'où me viendra mon secours.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 Le secours me viendra du Seigneur, qui a créé le ciel et la terre.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 Il ne fera point trébucher ton pied; celui qui te garde ne s'endormira pas.
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 Il ne sommeillera pas, il ne s'endormira point celui qui garde Israël.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 Le Seigneur te gardera, le Seigneur sera ton abri; sur toi il étendra sa maison.
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 Le soleil ne te brûlera point pendant le jour, ni la lune pendant la nuit.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 Le Seigneur te préservera de tout mal; le Seigneur gardera ton âme.
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 Le Seigneur te gardera, que tu entres ou que tu sortes, dès maintenant et dans les siècles des siècles.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.

< Psaumes 121 >