< Psaumes 118 >
1 Alléluiah! Rendez gloire au Seigneur, parce qu'il est bon, et que sa miséricorde est éternelle.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Que la maison d'Israël dise qu'il est bon, et sa miséricorde éternelle.
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 Que la maison d'Aaron dise qu'il est bon, et sa miséricorde éternelle.
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 Que tous ceux qui craignent le Seigneur disent qu'il est bon, et sa miséricorde éternelle.
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 Dans la tribulation j'ai invoqué le Seigneur, et il m'a exaucé, et il m'a mis au large.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 Que le Seigneur soit mon champion, et je ne craindrai rien de ce que l'homme peut me faire.
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 Que le Seigneur soit mon champion, et moi je mépriserai mes ennemis.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 Mieux vaut se confier au Seigneur que se confier à l'homme.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 Mieux vaut espérer dans le Seigneur qu'espérer dans les princes.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 Toutes les nations m'avaient environné; mais, au nom du Seigneur, je les ai repoussées.
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 Elles m'avaient enfermé dans un cercle pour m'envelopper; mais, au nom du Seigneur, je les ai repoussées.
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 Elles se pressaient autour de moi comme des abeilles autour d'un rayon de miel; elles lançaient des flammes, comme des épines en feu; mais, au nom du Seigneur, je les ai repoussées.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 À leur choc j'ai craint de tomber, et le Seigneur m'a secouru.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 Le Seigneur est ma force et ma louange; c'est lui qui m'a sauvé.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 La voix de l'allégresse et du salut est sous les tentes des justes; la droite du Seigneur a fait œuvre de puissance.
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 La droite du Seigneur m'a élevé; la droite du Seigneur a fait œuvre de puissance.
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 Je ne mourrai point; mais je vivrai et je raconterai les œuvres du Seigneur.
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 Le Seigneur m'a châtié pour me corriger; mais il ne m'a point livré à la mort.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Ouvrez-moi les portes de la justice, et je les franchirai, et je rendrai gloire au Seigneur.
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 C'est la porte du Seigneur, c'est par elle que les justes entreront.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 Je te rendrai gloire, parce que tu m'as exaucé, et que tu as été mon salut.
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 La pierre que les constructeurs avaient rejetée est devenue la pierre angulaire de l'édifice.
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 C'est le Seigneur qui a fait cela, et nos yeux en sont émerveillés.
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 Voici le jour qu'a fait le Seigneur; tressaillons et réjouissons-nous en ce jour.
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 Seigneur, sauve-moi; Seigneur, fais-moi prospérer.
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Béni soit celui qui vient au nom du Seigneur. Nous vous avons bénis de la maison du Seigneur.
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 Dieu, c'est le Seigneur; il a brillé à nos yeux: célébrez une fête solennelle avec des rameaux touffus, et ombragez jusqu'aux cornes de l'autel.
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 Tu es mon Dieu, et je te rendrai gloire; tu es mon Dieu, et je t'exalterai; je te rendrai gloire, parce que tu m'as exaucé, et que tu as été mon salut.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 Rendez gloire au Seigneur, parce qu'il est bon, et que sa miséricorde est éternelle.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.