< Psaumes 116 >

1 Alléluiah! J'ai aimé, parce que le Seigneur exaucera la voix de ma prière;
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Parce qu'il a incliné vers moi son oreille, et tous les jours de ma vie je l'invoquerai.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Les douleurs de la mort m'avaient environné; les périls de l'enfer m'avaient atteint. J'avais trouvé la souffrance et la tribulation; (Sheol h7585)
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
4 Et j'ai invoqué le nom du Seigneur. Seigneur, délivre mon âme!
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Le Seigneur est juste et compatissant, et notre Dieu fait miséricorde.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 Le Seigneur garde les petits; j'avais été humilié, et il m'a sauvé.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 O mon âme, retourne à ton repos, car le Seigneur a été bon pour toi.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Il a délivré mon âme de la mort, mes yeux des larmes, et mes pieds de la chute.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 Je me complairai en présence du Seigneur, en la terre des vivants.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 Alléluiah! J'ai cru, c'est pourquoi j'ai parlé; et j'avais été humilié à l'excès.
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 Or j'ai dit en mon extase: Tout homme est menteur.
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 Que rendrai-je au Seigneur pour tous les biens qu'il m'a faits?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Je prendrai le calice du salut, et j'invoquerai le nom du Seigneur.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 La mort de ses saints est précieuse aux yeux du Seigneur.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 La mort de ses saints est précieuse aux yeux du Seigneur.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Seigneur, je suis ton serviteur, je suis ton serviteur et le fils de ta servante; tu as rompu mes liens.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 Je te ferai un sacrifice de louanges, et j'invoquerai le nom du Seigneur.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Je rendrai mes vœux au Seigneur en face de tout son peuple,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 Dans les parvis du Seigneur, au milieu de tes murs, ô Jérusalem!
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psaumes 116 >