< Psaumes 115 >

1 Non pas à nous, Seigneur, non pas à nous, mais à ton nom, donnez-en la gloire,
Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 A cause de ta miséricorde et de ta vérité; de peur que les Gentils ne viennent à dire: Où est leur Dieu?
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
3 Notre Dieu est dans le ciel et sur la terre; tout ce qu'il a voulu, il l'a fait.
Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 Les idoles des Gentils sont argent et or, œuvres de la main des hommes.
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
5 Elles ont une bouche, et ne parleront pas; elles ont des yeux, et ne verront pas.
Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
6 Elles ont des oreilles, et n'entendront pas; elles ont des narines, et ne sentiront pas.
makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 Elles ont des mains, et ne toucheront pas; elles ont des pieds, et ne marcheront pas, et nul cri ne sortira de leur gosier.
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 Que ceux qui les font leur deviennent semblables, et tous ceux qui croient en elles.
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 La maison d'Israël a espéré dans le Seigneur, il est son champion et son appui.
Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 La maison d'Aaron a espéré dans le Seigneur, il est son champion et son appui.
Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Ceux qui craignent le Seigneur ont espéré dans le Seigneur; il est leur champion et leur appui.
Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 Le Seigneur s'est souvenu de nous, et nous a bénis; il a béni la maison d'Israël, il a béni la maison d'Aaron.
Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 Il a béni ceux qui craignent le Seigneur, les petits aussi bien que les grands.
adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
14 Que le Seigneur fasse plus encore pour vous, pour vous et pour vos enfants.
Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 Soyez bénis du Seigneur, qui a fait le ciel et la terre.
Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Le ciel des cieux est au Seigneur; mais la terre il l'a donnée aux fils des hommes.
Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 Les morts, Seigneur, ne te loueront point ni tous ceux qui descendent en enfer. (questioned)
Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
18 Mais nous qui vivons, nous bénirons le Seigneur, maintenant, et dans tous les siècles.
ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.

< Psaumes 115 >