< Psaumes 111 >
1 Alléluiah! Seigneur Dieu, je te rendrai gloire de tout mon cœur, dans le conseil et l'assemblée des justes.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 Les œuvres du Seigneur sont grandes et parfaites, selon toutes ses volontés.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 Son œuvre est digne d'actions de grâces et de gloire; sa justice durera dans tous les siècles des siècles.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Il a perpétué le mémorial de ses merveilles; le Seigneur est compatissant et miséricordieux.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 Il a donné la nourriture à ceux qui le craignent; il se souviendra éternellement de son alliance.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 Il a fait connaître à son peuple la vertu de ses œuvres,
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 Pour lui donner l'héritage des Gentils; les œuvres de ses mains sont vérité et jugement.
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 Tous ses commandements sont stables et fidèles dans tous les siècles, pleins de vérité et de droiture.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 Il a envoyé la rédemption à son peuple; il a intimé son alliance pour toujours; son nom est saint et redoutable.
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 La crainte du Seigneur est le commencement de la sagesse; l'intelligence en est donnée à tous ceux qui la pratiquent; on le louera dans tous les siècles des siècles.
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.