< Psaumes 1 >
1 Heureux l'homme qui n'est point allé au conseil des impies qui ne s'est pas arrêté dans la voie des pécheurs et ne s'est point assis dans la chaire de pestilence,
Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
2 Mais dont la volonté est conforme à la loi du Seigneur, et qui, nuit et jour, méditera sur cette loi.
Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
3 Il sera comme l'arbre planté au bord des eaux, et qui donnera son fruit en sa saison; ses feuilles ne tomberont jamais, et en toutes ses œuvres il prospérera.
Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
4 Ils ne sont pas ainsi les impies, ils ne sont pas ainsi; mais ils sont comme la paille que le vent balaie sur la face de la terre.
Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
5 C'est pourquoi les impies ne ressusciteront pas dans le jugement, ni les pécheurs dans l'assemblée des justes.
Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
6 Car le Seigneur connaît la voie des justes; et la voie des pécheurs périra.
Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.