< Proverbes 31 >

1 Ces paroles de moi ont été dites par Dieu; elles sont l'oracle du roi que sa mère a instruit.
Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 Enfant, que garderas-tu? Quoi? La parole de Dieu. Mon fils premier-né, que me reste-t-il à te dire, enfant de mes entrailles, enfant de mes yeux?
Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
3 Ne donne point aux femmes ta richesse, ta pensée et ta vie, de peur d'un remords tardif;
Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
4 fais tout avec prudence; bois du vin avec mesure. Les princes sont irascibles; qu'ils ne boivent point de vin,
Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
5 de peur qu'en buvant ils n'oublient la sagesse, et ne puissent plus juger les pauvres avec droiture.
kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
6 Enivrez les affligés; donnez du vin à boire à ceux qui souffrent;
Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
7 afin qu'ils oublient leur pauvreté, et ne se souviennent plus de leurs peines.
amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
8 Ouvre la bouche à la parole de Dieu, et rends justice à tous.
Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
9 Ouvre la bouche et juge selon l'équité, et plaide la cause du pauvre et du faible.
Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
10 Une femme forte, qui la trouvera? Une telle femme a plus de prix que les pierres précieuses.
Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 Le cœur de son mari a confiance en elle; jamais une telle femme n'aura besoin de recourir aux riches dépouilles d'un ennemi.
Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 Car elle emploie toute sa vie au bien de son époux.
Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 Elle dévide le lin et la laine, et elle fait de ses mains d'utiles travaux.
Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 Elle est comme un navire qui arrive de loin chargé de vivres;
Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
15 elle se lève avant le jour pour donner sa provende à la maison, et leur tâche à ses servantes.
Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 Elle a considéré le champ, et l'a acheté; et, dans cette propriété, elle sème des graines que ses mains ont recueillies.
Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 Elle ceint fortement ses reins, et met à l'œuvre toute la force de ses bras.
Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 Elle sait par expérience que le travail est bon, et sa lampe ne s'éteint pas de toute la nuit.
Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 Elle étend les bras partout où il est utile, et ses mains ne quittent pas le fuseau.
Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 Elle a la main ouverte pour le pauvre, et présente un fruit au mendiant.
Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 Son mari n'a pas à s'inquiéter des gens de sa maison, quel que soit le lieu où il est retenu; car elle a vêtu tous ceux qui sont auprès d'elle.
Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 Elle a fait pour son mari des manteaux doubles, et pour elle-même des manteaux de fin lin et de pourpre.
Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 Son mari est considéré devant les portes de la ville, lorsqu'il siège au conseil avec les anciens de la terre.
Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 Elle fait des toiles de fin lin; elle vend des ceintures aux Chananéens.
Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 Elle ouvre la bouche avec prudence et mesure; elle a mis un frein à sa langue.
Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 Elle s'est revêtue de force et de beauté, et goûte une douce joie dans ses derniers jours.
Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 Les habitudes de sa maison sont réglées; elle ne mange point les fruits de la paresse.
Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 Elle ouvre la bouche sagement et selon la loi. Elle a élevé ses enfants avec tendresse, et ils se sont enrichis; et son époux a fait son éloge
Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 beaucoup de filles ont acquis des richesses, beaucoup ont été vertueuses; mais toi, tu es au-dessus d'elles, tu les as toutes surpassées.
“Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
30 Les grâces sont trompeuses, et la beauté de la femme est vanité; mais la femme intelligente sera bénie, et celle qui craint le Seigneur sera louée.
Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 Donnez-lui les fruits de ses lèvres, et que son époux soit loué aux portes de la ville.
Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.

< Proverbes 31 >