< Proverbes 30 >

1 Ô mon fils, révère mes paroles; recueille-les et repens-toi. Voici ce que dit un homme à ceux qui se confient en Dieu; mais je m'arrête,
Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
2 car je suis moi-même le plus insensé des hommes, et la sagesse des mortels n'est point en moi
“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
3 mais Dieu m'a enseigné la sagesse, et je connais la doctrine des saints.
Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
4 Qui donc est monté au ciel et en est descendu? Qui a rassemblé les vents dans un pli de Son manteau? Qui a contenu les eaux comme dans un vêtement? Qui a pouvoir sur les extrémités de la terre? Quel est Son Nom? Quel est le nom de Ses enfants?
Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
5 Toutes les paroles de Dieu sont des flammes, et Il protège ceux qui Le craignent.
“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
6 N'ajoute rien à Ses paroles, de peur qu'Il ne te reprenne et ne t'accuse de mensonge.
Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
7 Seigneur, je Te demande deux choses: Ne me retire pas Ta grâce avant que je meure;
“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
8 éloigne de moi les paroles vaines et le mensonge; ne me donne ni la richesse ni la pauvreté; mais accorde-moi ce qui m'est nécessaire et suffisant;
Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
9 de peur que, rassasié, je ne devienne trompeur, et ne dise: Qui me voit? ou que, poussé par le besoin, je ne dérobe, et que je ne parjure le Nom du Seigneur.
kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
10 Ne livre pas l'esclave fugitif à son maître; de peur qu'il ne te maudisse, et que tu ne périsses à ton tour.
“Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
11 Une race pervertie maudit son père, et ne bénit pas sa mère.
“Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
12 Une race pervertie s'estime juste, et qui pourtant n'a point lavé le devant de sa porte.
Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
13 Une race pervertie a les yeux hautains; l'orgueil est sur ses paupières.
Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
14 D'une race pervertie les dents sont des glaives; et ses mâchoires, des couteaux pour détruire et dévorer, sur la terre, les humbles et les pauvres parmi les hommes.
Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
15 La sangsue avait trois filles qu'elle aimait d'un tendre amour; et à elles trois, elles ne remplissaient pas son cœur; une quatrième ne suffit pas pour lui faire dire: C'est assez.
“Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
16 L'enfer, l'amour d'une femme, une terre qui manque d'eau, l'eau et le feu ne diront jamais: C'est assez. (Sheol h7585)
Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol h7585)
17 L'œil qui se moque d'un père et qui n'honore point la vieillesse d'une mère, que les corbeaux du vallon l'arrachent, et que les aiglons le dévorent.
Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
18 Il y a trois choses qu'il m'est impossible de comprendre, et une quatrième que j'ignore
Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
19 la trace d'un aigle dans les airs, celle d'un serpent dans les rochers, les sentiers d'un ruisseau qui vogue sur l'eau, et les voies d'un homme dans sa jeunesse.
Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
20 Telle est la voie de la femme adultère, qui, après ce qu'elle a fait, se lave, et dit n'avoir rien fait d'inconvenant.
Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
21 Trois choses troublent la terre; il en est une quatrième qu'elle ne peut supporter
Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
22 un esclave devenu roi; un insensé regorgeant de biens;
Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
23 une servante qui a supplanté sa maîtresse, et une méchante femme réunie à un bon mari.
mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
24 Il y a sur la terre quatre êtres bien petits, et ils sont plus sages que les sages
Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
25 la fourmi, qui n'a point de force, et prépare en été sa nourriture;
Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
26 le hérisson, peuple débile, qui fait sa demeure sur les rochers;
mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
27 la sauterelle, qui n'a point de roi et marche comme une armée en bon ordre, au commandement d'une seule;
dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
28 et le lézard moucheté, qui se tient droit, et, quoique facile à prendre, habite les forteresses des rois.
Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
29 Il y a trois êtres dont la démarche est belle, et un quatrième dont le maintien est majestueux
“Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
30 le lionceau, le plus fort des animaux, qui ne recule devant rien, et ne redoute aucune bête;
Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
31 le coq, qui se promène, plein d'ardeur, parmi les poules; et le bouc qui conduit le troupeau, et le roi qui gouverne une nation.
Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
32 Si tu t'es laissé aller à la joie, et que tu étendes les mains pour te disculper, tu seras confondu.
“Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
33 Trais le lait avec trop de force, il deviendra du beurre; blesse-toi les narines, il en sortira du sang; cherche querelle, il s'ensuivra des rixes et des procès.
Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”

< Proverbes 30 >