< Proverbes 26 >

1 Il y a des rosées pendant la moisson, et des pluies pendant l'été; mais il n'est point de gloire pour l'insensé.
Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 Les oiseaux s'envolent et même les autruches: ainsi les vanités s'évanouissent sans arriver à rien.
Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 Comme est le fouet au cheval, l'aiguillon à l'âne, ainsi est la verge à une nature déréglée.
Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 Ne réponds point au fou selon sa folie, de peur que tu ne deviennes semblable à lui.
Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 Mais réponds au fou selon sa folie, de peur qu'il ne semble sage à tes dépens.
Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 Celui qui envoie ses paroles par un messager imprudent expose ses propres voies à un affront.
Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 Interdis aux insensés l'usage de leurs jambes, et empêche l'iniquité de sortir de leur bouche.
Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 Celui qui attache la pierre à sa fronde ressemble à celui qui glorifie un insensé.
Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 Des épines poussent dans la main d'un homme ivre, et la servitude dans la main des insensés.
Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 La chair des insensés est pleine de trouble; car leurs passions se brisent dans leur choc.
Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 Comme le chien, lorsqu'il revient à son vomissement, inspire le dégoût; ainsi est l'insensé qui, en sa malice, retourne à son péché. Il est une honte qui conduit au mal; il est une honte pleine de gloire et de grâce.
Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 J'ai vu un homme qui, lui-même, s'estimait sage; cependant l'insensé a plus de confiance que lui.
Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 Le paresseux que l'on envoie en voyage dit: Il y a un lion sur le chemin et des assassins dans les rues.
Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 Comme la porte tourne sur ses gonds, ainsi fait le paresseux sur son lit.
Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 Le paresseux, s'il a caché sa main sous son manteau, n'aura pas le courage de la porter à sa bouche.
Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 Le paresseux se croit plus sage que celui qui rapporte une dépêche et en reçoit un salaire abondant.
Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 Se mettre en avant pour la querelle d'autrui, c'est comme prendre un chien par la queue.
Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
18 On lance parmi les hommes des paroles comme des traits; celui qu'elles atteignent le premier succombe.
Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 C'est ce qui arrive à tous ceux qui dressent des embûches à leurs amis; et si l'on s'en aperçoit, ils disent: Je l'ai fait en jouant.
ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 Le feu s'active, s'il y a beaucoup de bois; où il n'y a point de contradicteur, les querelles s'apaisent.
Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 Le charbon et le bois dans le foyer animent le feu; le médisant entretient le trouble des querelles.
Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 Les paroles du trompeur sont douces; mais elles blessent jusqu'au fond des entrailles.
Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 L'argent donné pour tromper ne vaut pas mieux qu'un coquillage. Des lèvres frivoles cachent un mauvais cœur.
Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 Un ennemi que l'on voit pleurer promet beaucoup des lèvres; mais en son cœur il trame quelque fraude.
Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 Si ton ennemi te prie à grands cris, ne te laisse pas persuader; car il a sept méchancetés dans l'âme.
Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 Celui qui dissimule sa haine cherche à tromper; mais il a beau cacher ses fautes, le monde le connaît bien.
Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 Celui qui creuse une fosse pour son prochain y tombera; celui qui roule une pierre la roule sur lui-même.
Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 Une langue trompeuse hait la vérité; une bouche indiscrète est une cause de ruines.
Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.

< Proverbes 26 >