< Proverbes 24 >

1 Mon fils, ne rivalise point avec les méchants, et ne désire pas être avec eux.
Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
2 Car leur cœur médite des fraudes, et leurs lèvres disent des paroles affligeantes.
pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
3 La sagesse bâtit sa maison; l'intelligence la dirige;
Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
4 avec la doctrine on remplit les celliers de tout ce qu'il y a de riche, de précieux et de bon.
Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
5 Mieux vaut le sage que le fort, et un homme de bon sens que de vastes domaines.
Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
6 Avec l'art de gouverner, on conduit la guerre; avec un cœur résolu, on trouve le salut.
Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
7 La sagesse et les bonnes pensées sont à la porte des sages; les sages ne se détournent pas de la parole du Seigneur.
Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
8 Mais ils sont appréciés dans les conseils. la mort surprend les imprudents.
Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
9 L'insensé meurt dans son péché. L'impureté est dans l'homme de pestilence;
Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
10 il sera déshonoré au jour fatal, au jour de la tribulation, jusqu'à ce qu'il soit renversé.
Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
11 Délivre ceux que l'on conduit à la mort; rachète ceux qu'on va faire mourir, et n'y épargne pas tes soins.
Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
12 Si tu dis: Je ne connais pas cet homme; sache que Dieu connaît tous les cœurs; Celui qui a donné le souffle à tous, sait toutes choses, et Il rétribue chacun selon ses œuvres.
Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
13 Mon fils, mange du miel; car le rayon de miel est bon; que ton gosier en goûte la douceur.
Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
14 C'est ainsi que tu feras comprendre la sagesse à ton âme; car si tu l'acquiers, ta fin sera bonne, et l'espérance ne t'abandonnera point.
Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
15 Ne conduis pas l'impie dans les pâturages des justes; ne te laisse pas séduire par l'appât de la gourmandise.
Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
16 Car le juste tombera sept fois, et il se relèvera; mais les impies seront sans force dans le malheur.
paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
17 Si ton ennemi tombe, ne te moque pas de lui, et ne t'enorgueillis pas de sa ruine.
Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
18 Car le Seigneur te verrait, et Il ne t'aurait point pour agréable, et Il détournerait Sa colère de ton ennemi.
Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
19 Ne prends point part aux joies des méchants; ne porte point envie aux pécheurs.
Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
20 Car les pervers n'auront point de postérité, et la langue des impies s'éteindra.
paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
21 Crains Dieu et le roi, mon fils, et ne leur désobéis jamais.
Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
22 Car ils punissent inopinément les impies; et qui peut prévoir quelle sera leur vengeance?
awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
23 Qu'aucun mensonge se soit dit par la langue du roi; que nulle fausseté ne sorte de sa langue. Voici ce que je dis, à vous sages, pour que vous le sachiez: Il n'est pas bien, en justice, d'avoir égard au rang.
Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
24 La langue du roi n'est point de chair, c'est un glaive; et celui qui lui sera livré, sera brisé; Ceux qui disent de l'impie: C'est un juste, seront maudits du peuple et odieux aux nations.
Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
25 car si sa colère est excitée, elle détruit les hommes avec leurs nerfs; Mais ceux qui le réprimandent paraîtront meilleurs, et la bénédiction viendra sur eux.
Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
26 elle dévore leurs os, elles les consume comme la flamme, au point que les aiglons n'y trouveraient pas de quoi se repaître. On baisera les livres qui diront de bonnes paroles.
Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
27 Prépare ton ouvrage au dehors; arrive à ton champ, tout préparé; marche sur mes traces, et tu réédifieras ta maison.
Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
28 Ne porte pas contre un concitoyen de faux témoignage, et n'ouvre pas les lèvres contre lui.
Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
29 Ne dis pas: Comme il m'a traité, je le traiterai; je me vengerai du tort qu'il m'a fait.
Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
30 L'insensé est comme un champ; l'homme qui manque d'esprit est comme un vignoble.
Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
31 Si tu le délaisses, il sera stérile et tout couvert de mauvaises herbes; il dépérit, et sa clôture de pierres s'écroule.
Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
32 À la fin, j'ai réfléchi et j'ai songé à chercher la vraie doctrine.
Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
33 Je sommeille un moment; un moment je m'endors, et je me tiens un moment les bras croisés.
Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
34 Si tu fais cela, l'indigence t'arrivera à grands pas, et le besoin fondra sur toi comme un agile coursier.
umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.

< Proverbes 24 >