< Proverbes 23 >

1 Si tu t'assieds pour dîner à la table d'un prince, fais bien attention à ce qui te sera présenté
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 puis étends la main, sachant qu'il convient qu'on te serve de tels mets; toutefois, même si tu as grand appétit,
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 ne convoite point leur repas; car c'est là une vie factice.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Si tu es pauvre, n'aspire pas à la richesse; repousse-la même en pensée.
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 Si tu fixes ton regard sur elle, tu la vois disparaître; car elle a, comme l'aigle, des ailes prêtes à s'envoler, et retourne à la maison de son premier maître.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Ne dîne pas avec un homme envieux; ne désire rien de sa table;
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 car il mange et il boit comme on avalerait un cheveu. Ne l'introduis pas chez toi, et ne mange pas un morceau avec lui;
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 car il le vomirait et souillerait tes meilleures paroles.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Ne dis rien à l'insensé, de peur que peut-être il ne tourne en dérision tes sages discours.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Ne dépasse pas les bornes anciennes, et n'entre pas dans le champ de l'orphelin;
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 car il est fort celui que le Seigneur rachète; et, si tu es en procès avec lui, Dieu plaidera sa cause.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Livre ton cœur à la discipline, et prépare ton oreille aux paroles de la doctrine.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Ne cesse de corriger un enfant; car si tu le frappes de verges, il n'en mourra pas.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Et si tu le frappes de verges, tu sauveras son âme de la mort. (Sheol h7585)
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
15 Mon fils, si ton cœur est sage, tu réjouiras aussi mon cœur;
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 et si tes lèvres sont droites, elles converseront avec mes lèvres.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Que ton cœur ne porte point envie aux pécheurs; mais sois toujours dans la crainte de Dieu.
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 Car si tu observes ces choses, tu auras des descendants, et ton espérance ne sera pas trompée.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Écoute, mon fils, et sois sage; et maintiens droites les pensées de ton cœur.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Ne sois pas buveur de vin; évite les longs banquets et la profusion des viandes.
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 Car l'ivrogne et le débauché mendieront; le paresseux sera revêtu de haillons en lambeaux.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Écoute, mon fils, le père qui t'a engendré, et ne méprise pas ta mère parce qu'elle a vieilli.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 Un père juste élève bien ses enfants, et la sagesse d'un fils réjouit son âme.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Que ton père et ta mère se réjouissent en toi, et que celle qui t'a enfanté soit heureuse.
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 Mon fils, donne-moi ton cœur; que tes yeux gardent mes voies.
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 La maison étrangère est comme un tonneau percé; il est étroit le puits de l'étranger.
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Celui qui les recherche périra bientôt, et tout pécheur sera détruit.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Pour qui les gémissements? Pour qui le trouble? Pour qui les contestations? Pour qui les ennuis et les entretiens frivoles? Pour qui les repentirs inutiles? Pour qui les yeux livides?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 N'est-ce pas pour ceux qui passent leur temps dans l'ivresse et qui hantent les lieux où l'on boit?
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Ne vous enivrez pas; mais faites votre société des hommes justes, et fréquentez-les publiquement. Car si vos yeux s'arrêtent sur les fioles et les coupes, plus tard vous marcherez plus nu qu'un pilon à mortier.
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 L'homme ivre finit par s'étendre comme si un serpent l'avait mordu; le venin se répand sur lui comme de la dent d'un reptile.
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Si tes yeux regardent une femme étrangère, la langue aussitôt divaguera,
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 et tu seras gisant comme au sein de la mer, et comme un pilote au milieu de l'orage.
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 Et tu diras: On m'a frappé, et je n'en ai pas souffert; on s'est joué de moi, et je ne m'en suis pas douté; quand viendra l'aurore, pour m'en aller encore chercher des hommes avec qui je puisse me retrouver?
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”

< Proverbes 23 >