< Proverbes 18 >
1 L'homme qui veut rompre avec ses amis cherche des prétextes, et en tout temps il sera digne de blâme.
Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
2 Celui qui manque de sens n'a que faire de la sagesse; il est plutôt conduit par la folie.
Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
3 Lorsque l'impie est tombé en un abîme de fautes, il n'en tient compte; mais la honte et les ignominies lui arrivent.
Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
4 La parole dans le cœur de l'homme est une eau profonde; un fleuve en jaillit, et une fontaine de vie.
Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
5 Il n'est pas bien d'avoir égard à la parole de l'impie; se détourner de l'équité dans la jeunesse est une impiété.
Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
6 Les lèvres de l'insensé le mènent à mal, et sa bouche hardie appelle la mort.
Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
7 La bouche de l'insensé est sa ruine; ses lèvres sont un piège pour son âme.
Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
8 La crainte abat les paresseux; les âmes des efféminés sont toujours affamées.
Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
9 Qui n'a point d'ardeur en ses travaux est frère de celui qui se détruit lui-même.
Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
10 Le Nom du Seigneur est d'une force toute-puissante; les justes qui courent à Lui sont glorifiés.
Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
11 Les biens du riche sont une forteresse; sa gloire projette au loin de l'ombre.
Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
12 Le cœur de l'homme s'exalte avant d'être brisé; ils s'humilie avant d'être glorifié.
Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
13 Répondre avant d'avoir entendu, c'est insensé et blâmable.
Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
14 Un serviteur prudent apaise la colère de l'homme; qui peut supporter un homme pusillanime?
Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
15 Le cœur de l'homme sensé possède la doctrine; les oreilles du sage cherchent l'intelligence.
Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
16 Les présents que fait un homme le grandissent et le font siéger parmi les puissants.
Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
17 Le juste s'accuse le premier; mais s'il est ensuite attaqué, c'est son adversaire qu'on blâme.
Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
18 L'homme silencieux apaise les contradictions; il juge entre les puissants.
Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
19 Un frère, soutenu par son frère, est comme une puissante et haute cité; il est fort comme un palais solidement bâti.
Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
20 L'homme remplit ses entrailles des fruits de sa bouche, et se rassasiera du fruit de ses lèvres.
Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
21 La mort et la vie sont au pouvoir de la langue; ceux qui la maîtrisent mangeront ses fruits.
Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
22 Celui qui a trouvé une femme bonne a trouvé des grâces; il a reçu de Dieu l'allégresse. Celui qui répudie une femme bonne répudie une bonne fortune; celui qui garde une adultère est impie et insensé.
Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.