< Nombres 2 >

1 Le Seigneur parla ensuite à Moïse, disant:
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
2 Que les fils d'Israël campent en face les uns des autres, chaque homme restant à son rang sous ses enseignes, avec sa maison paternelle; qu'ils campent autour du tabernacle du témoignage.
“Aisraeli azimanga misasa yawo mozungulira tenti ya msonkhano motalikira pangʼono. Munthu aliyense amange pamene pali mbendera ya fuko lake.”
3 Les premières tentes du côté de l'orient seront sous le commandement du camp de Juda, avec leur armée, et le chef des fils de Juda sera Nahasson, fils d'Aminadab.
Kummawa, kotulukira dzuwa, magulu a msasa wa Yuda amange pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Ayudawo ndi Naasoni mwana wa Aminadabu.
4 Son armée, selon le recensement, est de soixante-quatorze mille six cents hommes.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 74,600.
5 A côté, campera la tribu d'Issachar; leur chef sera Nathanaël, fils de Sogar.
Fuko la Isakara lidzamanga pafupi ndi Yuda. Mtsogoleri wa gulu la Isakara ndi Netanieli mwana wa Zuwara.
6 Son armée, selon le recensement, est de cinquante-quatre mille quatre cents hommes.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 54,400.
7 A côté, campera la tribu de Zabulon; leur chef sera Eliab, fils de Chaïlon.
Lotsatira lidzakhala fuko la Zebuloni. Mtsogoleri wa gulu la Zebuloni ndi Eliabu mwana wa Heloni.
8 Son armée selon le recensement, est de cinquante-sept mille quatre cents hommes.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 57,400.
9 Tous les hommes recensés du camp de Juda forment un corps de cent quatre- vingt-six mille quatre cents hommes; ils lèveront le camp les premiers avec toutes leurs forces.
Anthu onse aamuna mʼmisasa ya Yuda, chiwerengero chawo ndi 186,400 monga mwa magulu awo. Iwowo ndiwo aziyamba kusamuka.
10 Le camp de Ruben se rangera du côté du midi; et le chef des fils de Ruben sera Elisur, fils de Sédiur.
Kummwera kudzakhala magulu a msasa wa Rubeni pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu la Rubeni ndi Elizuri mwana wa Sedeuri.
11 Son armée, selon le recensement, est de quarante-six mille cinq cents hommes.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 46,500.
12 A côté, campera la tribu de Siméon; leur chef sera Salamiel, fils de Surisadaï.
Fuko la Simeoni lidzamanga pafupi ndi Rubeni. Mtsogoleri wa gulu la Simeoni ndi Selumieli mwana wa Zurisadai.
13 Son armée, selon le recensement, est de cinquante-neuf mille trois cents hommes.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 59,300.
14 A côté, campera la tribu de Gad; leur chef sera Eliasaph, fils de Raguel.
Lotsatira lidzakhala fuko la Gadi. Mtsogoleri wa gulu la Gadi ndi Eliyasafu mwana wa Deuweli.
15 Son armée, selon le recensement, est de quarante-cinq mille six cent cinquante hommes.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 45,650.
16 Tous les hommes recensés du camp de Ruben, forment un corps de cent cinquante-un mille trois cent cinquante hommes; ils décamperont les seconds avec toutes leurs forces.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Rubeni, chiwerengero chawo monga mwa magulu awo, ndi 151,450. Iwowo azikhala achiwiri posamuka.
17 Le tabernacle du Seigneur sera dressé, et le camp des lévites sera placé au centre des camps; on marchera dans le même ordre que l'on dressera les tentes, chacun restant au corps auquel il appartient.
Tsono tenti ya msonkhano ndi msasa wa Alevi zidzakhala pakati pa misasayo. Iwo adzasamuka monga momwe anamangira misasa yawo, aliyense pa malo ake pamene pali mbendera yake.
18 Le camp d'Ephraïm se rangera du côté de l'occident; le chef des fils d'Ephraïm sera Elisama, fils d'Emiud.
Kumadzulo kudzakhala magulu a msasa wa Efereimu pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Aefereimuwo ndi Elisama mwana wa Amihudi.
19 Son armée, selon le recensement, est de quarante mille cinq cents hommes.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 40,500.
20 A côté, campera la tribu de Manassé; leur chef sera Gamaliel, fils de Phadasur.
Fuko la Manase lidzakhala pafupi ndi Efereimu. Mtsogoleri wa Amanase ndi Gamalieli mwana wa Pedazuri.
21 Son armée, selon le recensement, est de trente-deux mille deux cents hommes.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 32,200.
22 A côté, campera la tribu de Benjamin; leur chef sera Abidan, fils de Gadéoni.
Lotsatira lidzakhala fuko la Benjamini. Mtsogoleri wa Abenjamini ndi Abidani mwana wa Gideoni.
23 Son armée, selon le recensement, est de trente-cinq mille quatre cents hommes.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 35,400.
24 Tous les hommes recensés du camp d'Ephraïm forment un corps de cent huit mille cent hommes; ils décamperont avec toutes leurs forces.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Efereimu, chiwerengero chawo ndi 108,100 monga mwa magulu awo. Iwowo azikhala achitatu posamuka.
25 Le camp de Dan se rangera du côté du nord; et le chef des fils de Dan sera Achiézer, fils d'Amisadaï.
Kumpoto kudzakhala msasa wa magulu a Dani pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Adani ndi Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
26 Son armée, selon le recensement, est de soixante-deux mille sept cents hommes.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 62,700.
27 A côté, campera la tribu d'Aser; leur chef sera Phagéel, fils d'Echran.
Fuko la Aseri lidzamanga pafupi ndi iwowo. Mtsogoleri wa Aaseri ndi Pagieli mwana wa Okirani.
28 Son armée, selon le recensement, est de quarante-un mille cinq cents hommes.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 41,500.
29 A côté, campera la tribu de Nephthali; leur chef sera Achire, fils d'Enan.
Lotsatira lidzakhala fuko la Nafutali. Mtsogoleri wa Anafutali ndi Ahira mwana wa Enani.
30 Son armée, selon le recensement, est de cinquante-trois mille quatre cents hommes.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 53,400.
31 Tous les hommes recensés du camp de Dan forment un corps de cent cinquante-sept mille six cents hommes; ils décamperont les derniers, selon leur rang.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Dani chiwerengero chawo ndi 157,600. Iwo azidzanyamuka pomaliza, ndi mbendera zawo.
32 Tel est le dénombrement des fils d'Israël, par maisons paternelles; le total du recensement de leurs forces donne six cent trois mille cinq cent cinquante hommes.
Amenewa ndi Aisraeli monga mwa mabanja a makolo awo. Chiwerengero cha Aisraeli onse mʼmisasa chinali 603,550, mwa magulu awo.
33 Or, les lévites, comme le Seigneur l'avait prescrit à Moïse, ne furent point recensés avec eux.
Koma Alevi sanawawerenge pamodzi ndi Aisraeli enawo monga momwe Yehova analamulira Mose.
34 Et les fils d'Israël firent tout ce que le Seigneur avait prescrit à Moïse; ils campèrent dans l'ordre à eux assigné, ils marchèrent en continuant de se tenir les uns près des autres, rangés par familles et par tribus.
Choncho Aisraeli anachita zonse zomwe Yehova analamulira Mose. Umo ndi momwe amamangira misasa yawo pamene panali mbendera zawo, ndipo ankasamuka monga mwa mafuko a makolo awo.

< Nombres 2 >