< Néhémie 5 >

1 Et il y eut un grand cri du peuple et de leurs femmes, contre les Juifs leurs frères.
Tsono anthu ena ndi akazi awo anayamba kudandaula kwambiri chifukwa cha Ayuda anzawo.
2 Et les uns disaient: Nous sommes en grand nombre avec nos fils et nos filles, vendons-en; puis nous achèterons du blé, et nous mangerons, et nous vivrons.
Ena ankanena kuti, “Ife ndi ana athu aamuna ndi aakazi, tilipo ochuluka kwambiri. Choncho tikufuna tirigu kuti tidye ndi kukhala ndi moyo.”
3 Et d'autres disaient: Engageons nos champs, nos vignes, nos maisons; puis, nous achèterons du blé, et nous mangerons.
Panali ena amene ankanena kuti, “Ife tikuchita kupereka minda yathu, mitengo yathu ya mphesa ndi nyumba zathu ngati chikole kuti tipeze tirigu chifukwa njala yakula.”
4 D'autres encore disaient: Nous avons emprunté de l'argent pour les impôts du roi, sur nos champs, et nos vignes, et nos maisons.
Panalinso ena amene ankanena kuti, “ife tinachita kukongola ndalama zoti tipereke msonkho wa minda ndi mitengo yathu ya mphesa kwa mfumu.
5 Et maintenant, notre chair est comme la chair de nos frères; nos fils sont comme leurs fils, et nous traitons nos fils et nos filles comme des esclaves; et il y a de nos filles qui sont servantes, et nous n'avons pas le pouvoir de les racheter; car les nobles possèdent nos champs et nos vignes.
Ngakhale kuti ndife amodzi ndi abale athuwa, ndipo ngakhalenso ana athu ndi ofanana ndi ana awo, ife tikukakamiza ana athu kuti akhale akapolo. Ena mwa ana athu aakazi atengedwa kale ukapolo. Ife tilibe mphamvu yochitapo kanthu popeza anthu ena anatenga kale minda yathu ndi mitengo yathu ya mphesa.”
6 Et j'eus une grande affliction, quand j'ouïs leur clameur et ces discours;
Nditamva madandawulo awo ndi zimene amanenazi ndinapsa mtima kwambiri.
7 Et je tins conseil en mon cœur, et je combattis les nobles et les princes, et je leur dis: Un homme peut-il demander à son frère ce que vous demandez? Et je convoquai contre eux une grande assemblée.
Nditalingalira bwino ndinatsimikiza zoti ndichitepo kanthu ndipo kenaka ndinawadzudzula anthu olemekezeka ndi akuluakuluwo. Ndinawawuza kuti, “Zoona ndithu inu nʼkumalipiritsana chiwongoladzanja chachikulu anthu apachibale nokhanokha!” Choncho ndinayitanitsa msonkhano waukulu kuti ndiwazenge mlandu
8 Et je leur dis: Nous avons, de nos dons volontaires, racheté nos frères les Juifs qui avaient été vendus aux gentils, et vous vendez vos frères; mais vous seront-ils livrés? Et ils gardèrent le silence, et ils ne trouvèrent pas un mot à dire.
ndipo ndinati, “Monga zakhaliramu ife tikutha kuwombola abale anthu amene anagulitsidwa ukapolo kwa anthu ena. Kodi tsopano inu mukugulitsanso abale anu kwa anzawo kuti ife tiwumirizidwe kuwawombola?” Iwo anakhala chete, chifukwa sanapeze mawu oti anene.
9 Et je dis: Elle n'est pas bonne l'action que vous faites; ce n'est pas ainsi que vous vous soustrairez, par la crainte de Dieu, aux outrages des nations, vos ennemies.
Kotero ndinapitiriza kunena kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino. Kodi inu simungakhale ndi moyo woopa Mulungu wathu kuti tipewe kunyoza kwa adani athu, anthu a mitunda inayi?
10 Or, mes frères, mes parents et moi-même, nous leurs avons prêté de l'argent et du blé; eh bien! renonçons à rien exiger d'eux.
Ine ndi abale anga ndiponso antchito anga tikuwakongozanso anthuwa ndalama ndi tirigu. Ndipo tiyeni tilekeretu zolandira chiwongoladzanja!
11 Rendez-leur dès aujourd'hui leurs champs, leurs vignes, leurs oliviers et leurs maisons; et apportez-leur du blé, du vin et de l'huile pour prix de l'argent.
Abwezereni lero lomwe minda yawo, mitengo ya mphesa, mitengo ya olivi ndiponso nyumba zawo. Muwabwezerenso chiwongoladzanja cha ndalama, tirigu, vinyo ndi mafuta zimene munatenga.”
12 Et ils dirent: Nous rendrons tout; nous ne leur demanderons rien, et nous ferons ce que tu dis. Et j'appelai les prêtres, et je les adjurai de faire selon cette parole.
Iwo anayankha kuti, “Ife tidzawabwezera zimenezi popanda kupemphapo kanthu kalikonse kwa iwo. Tidzachita monga mwanena.” Pambuyo pake ndinayitanitsa ansembe ndipo pamaso pawo ndinawalumbiritsa atsogoleriwo ndi akuluakuluwo kuti adzachitadi zomwe analonjezazo.
13 Et je secouai mon manteau, et je dis: Que Dieu ainsi secoue hors de sa maison et de son jardin tout homme qui n'accomplira pas cette parole; que cet homme soit ainsi secoué et vide. Et toute l'Église dit: Amen. Et ils louèrent le Seigneur, et le peuple fit comme il avait été dit.
Ndipo inenso ndinakutumula chovala changa ndi kuti, “Chimodzimodzinso Mulungu akutumule munthu wosasunga malonjezano ake. Amulande nyumba yake ndi katundu wake ndi kumusandutsa mʼmphawi!” Apo msonkhano wonse unati, “Ameni” natamanda Yehova. Ndipo anthu aja anachita monga analonjezera.
14 Depuis le jour où le roi m'avait commandé d'être leur chef en la terre de Juda: de la vingtième à la trente-deuxième année du règne d'Arthasastha, pendant douze ans, ni moi ni mes frères nous ne mangeâmes de vivres extorqués d'eux.
Ndiponso kuyambira nthawi imene anandisankha kuti ndikhale bwanamkubwa wa dziko la Yuda, kuchokera chaka cha makumi awiri mpaka chaka cha 32 muulamuliro wa ufumu wa Aritasasita, ndiye kuti kwa zaka zokwana 12, ine ngakhale abale anga sitinalandire chakudya choyenerera bwanamkubwa.
15 Et toutes les extorsions dont mes devanciers les grevaient avant moi, leur avaient enlevé jusqu'à leur dernier argent; ils leur prenaient pour le pain et le vin quarante sicles par jour; et leurs agents avaient toute autorité sur le peuple; et moi je ne fis pas ainsi, en face de la crainte de Dieu.
Koma abwanamkubwa akale ankasautsa anthu. Iwo ankalanda anthu chakudya ndi vinyo ndi kuwalipiritsanso masekeli asiliva makumi anayi. Ngakhalenso antchito awo amavutitsa anthu kwambiri. Koma ine sindinachite zimenezo chifukwa ndimaopa Mulungu.
16 Et, pendant la réédification des murailles, je ne leur extorquai rien, je n'achetai point de champ, non plus qu'aucun de ceux que j'avais rassemblés pour cette œuvre.
Ndiponso ndinadzipereka kugwira ntchito yomanga khoma la mzinda wa Yerusalemu popanda ngakhale kugulapo munda. Antchito anganso anasonkhana komweko kuti agwire ntchito ndipo sitinafunenso malo ena.
17 Et les Juifs, au nombre de cent cinquante, et ceux des gentils qui venaient d'alentour auprès de nous, mangeaient à ma table.
Kuwonjezera apa, ndinkadyetsa Ayuda, akuluakulu kuphatikizanso anthu amene ankabwera kwa ife kuchokera kwa mitundu ya anthu otizungulira okwanira 150.
18 Et tous les jours on m'amenait un bœuf, six brebis de choix et un chevreau. Et, tous les dix jours, il me venait pour nous tous une ample provision de vin; et, avec tout cela, je ne pris jamais de vivres par extorsion, parce que la servitude avait été pesante pour le peuple.
Tsiku lililonse pamaphikidwa ngʼombe imodzi, nkhosa zabwino zisanu ndi imodzi pamodzi ndi nkhuku. Ndipo pakutha pa masiku khumi aliwonse pankakhala matumba achikopa ochuluka a vinyo wa mitundu yonse. Ngakhale zinali choncho, Ine sindinatenge chakudya choperekedwa kwa bwanamkubwa, chifukwa izi zinali zosautsa anthu.
19 Souvenez-vous de moi, mon Dieu, pour mon bien, à cause de tout ce que j'ai fait en faveur de ce peuple.
Kuti zinthu zindiyendere bwino, kumbukirani Yehova Mulungu wanga pa zonse zimene ndachitira anthu awa.

< Néhémie 5 >