< Néhémie 1 >

1 Récits de Néhémias, fils d'Helcias. Au mois de chaseleu, en la vingtième année, j'étais à Suse, résidence royale.
Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya: Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa,
2 Et Anani, l'un de mes frères, vint, lui et des hommes de Juda, et je les questionnai, tant sur ceux qui étaient demeurés de la captivité et vivaient encore, que sur Jérusalem.
Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.
3 Et ils me dirent: Ceux qui sont demeurés, et qui ont été laissés de la captivité, sont dans la terre promise en grande détresse et opprobre; les murs de Jérusalem ont été abattus, et ses portes brûlées par le feu.
Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”
4 Or, quand j'eus ouï de telles paroles, je m'assis et pleurai, et, pendant plusieurs jours, me lamentai, et j'étais jeûnant et priant devant le Dieu du ciel.
Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba.
5 Et je dis: Que cela ne soit, je vous prie, Seigneur Dieu du ciel, Dieu fort, grand et redoutable qui gardez votre alliance et votre miséricorde à ceux qui vous aiment et observent vos commandements.
Ndinkati: “Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu.
6 Que votre oreille soit attentive, que vos yeux s'ouvrent, afin d'ouïr l'oraison de votre serviteur que je fais maintenant devant vous, nuit et jour, pour vos serviteurs les enfants d'Israël; et je me confesse pour les péchés des enfants d'Israël, en lesquels nous avons péché contre vous. Moi et la maison de mon père avons péché.
Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani.
7 Nous avons rompu l'alliance; nous n'avons point gardé les commandements, les jugements et les ordonnances que vous avez intimés à Moïse, votre serviteur.
Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.
8 Souvenez-vous de la parole que vous avez intimée à Moïse, votre serviteur, disant: Si vous manquez à notre alliance, je vous disperserai parmi les nations.
“Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina.
9 Et si vous revenez à moi, si vous gardez mes commandements, si vous les pratiquez, quand vous seriez disséminés jusqu'aux lieux où la terre touche le ciel, je vous en ramènerai, je vous réunirai en la terre que j'ai choisie pour que mon nom y réside.
Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’
10 Et voici vos serviteurs et votre peuple que vous avez rachetés par votre toute-puissance et votre forte main.
“Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
11 Qu'ils ne demeurent pas ainsi, Seigneur; mais que votre oreille soit attentive à l'oraison de votre serviteur et à celle de vos serviteurs qui veulent craindre votre nom. Soyez-lui propice aujourd'hui à votre serviteur; faites qu'il trouve miséricorde devant les hommes; or, j'étais échanson du roi.
Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.” Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.

< Néhémie 1 >