< Nahum 2 >

1 Il est monté Celui qui délivre de l'affliction, te soufflant au visage. Observe la voie; ceins-toi les reins; agis en homme selon ta force.
Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
2 Le Seigneur a détourné l'outrage fait à Jacob, ainsi que l'outrage fait à Israël; car les envahisseurs les ont arrachés, et ils ont détruit leurs plantations.
Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
3 Ils ont détruit les armes qui les rendaient puissants parmi les hommes, et leurs vaillants qui se jouaient de la flamme; mais au jour de Sa venue, les rênes de leurs chars et leurs cavaliers seront en désordre.
Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
4 Dans les rues, les chars s'entrechoqueront; ils s'embarrasseront les uns les autres au milieu des places. leurs aspect sera comme des lampes de feu, ou des éclairs sillonnant la nue.
Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
5 Et leurs grands se souviendront alors, et ils fuiront le jour, et ils défailliront en leur chemin, et ils se hâteront de courir à leurs remparts, et ils y placeront des sentinelles.
Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
6 Mais les portes des villes ont été forcées, et les palais du roi ont croulé;
Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
7 et les fondations en ont été mises à découvert, et n'ont plus été qu'un monceau de ruines, et les femmes ont été emmenées comme des colombes, gémissant en leurs cœurs.
Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
8 Et les eaux de Ninive ont été comme un étang plein d'eau, et ses habitants ont fui, et ils ne s'y sont pas arrêtés, et pas un n'a regardé en arrière.
Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
9 Les vainqueurs ont pillé l'argent, ils ont pillé l'or; car ses ornements étaient sans nombre; ils sont accablés sous le poids des vases qu'elle avait convoités.
Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
10 Ce n'est partout que coups et contrecoups, tumulte et brisement du cœur, défaillance des genoux et violentes douleurs de reins; toute face est comme le fond noir d'une chaudière.
Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
11 Où est le repaire des lions, et le pâturage des lionceaux? Où est allé le lion pour que le lionceau y entre avec lui? Et n'y avait-il personne pour les effrayer?
Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
12 Le lion ravissait ce qui convenait à ses lionceaux, et pour eux il multipliait les meurtres; il remplissait de gibier son antre, et de rapines son repaire.
Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
13 Voilà que je viens à toi, dit le Seigneur tout-puissant, et Je brûlerai au milieu de la fumée ton peuple nombreux, et le glaive dévorera tes lions, et Je détruirai sur la terre le fruit de tes rapines, et l'on n'entendra plus parler de tes œuvres.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”

< Nahum 2 >