< Nahum 1 >

1 Prédiction à Ninive, livre de la vision de Nahum, Elcéséen.
Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
2 Dieu est jaloux, le Seigneur Se venge, le Seigneur Se venge avec colère, le Seigneur tire vengeance de ceux qui Lui sont opposés; Il extermine Ses ennemis.
Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
3 Le Seigneur est longanime, Sa force est grande; mais le Seigneur ne laissera pas impuni celui qu'Il n'a pas encore puni; Sa voie est dans la destruction et les ébranlements; et les nuages sont la poussière de Ses pieds.
Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
4 C'est Lui qui menace la mer et qui la dessèche; c'est Lui qui change en désert tous les fleuves. Basan et le Carmel ont défailli, et les fleurs du Liban se sont fanées.
Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
5 Par Lui, les montagnes ont tressailli et les collines ont tremblé; devant Sa face toute la terre a reculé, et ceux qui l'habitent
Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
6 Qui soutiendra le regard de Sa fureur? Qui résistera aux transports de Son courroux? Sa colère ronge les fondations; les rochers se fendent devant Lui.
Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
7 Le Seigneur est doux pour ceux qui L'attendent au jour de la tribulation; Il connaît ceux qui Le révèrent.
Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
8 Il détruira votre voie par une inondation; les ténèbres poursuivent ceux qui se lèvent contre Lui et Le haïssent.
koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
9 Pourquoi vos pensées sont-elles contre le Seigneur? Lui seul mène toutes choses à leur fin; Il ne S'y prendra pas à deux fois pour vous briser.
Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
10 Et celui-là sera dévasté jusqu'aux fondations, il sera dévoré par la flamme comme l'if aux rameaux entrelacés, comme le chaume tout à fait desséché.
Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
11 De toi, ô Ninive, sortira contre le Seigneur une pensée méchante et ennemie.
Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
12 Or voici ce que dit le Seigneur, souverain Maître des grandes eaux. Ils seront séparés pareillement, et l'on n'entendra plus parler de toi.
Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
13 Et maintenant, Mon peuple, Je vais briser loin de toi sa verge, et rompre tes liens.
Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
14 Voici ce que sur toi, Ninive, a prescrit le Seigneur: Ta renommée ne sera plus semée au loin; Je détruirai dans le temple de ton dieu les images sculptées ou jetées en fonte; Je vais comme en courant préparer ton sépulcre.
Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
15 Voici sur les montagnes les pieds de Celui qui apporte la bonne nouvelle et qui annonce la paix. Juda, célèbre tes fêtes, accomplis tes vœux, car tes ennemis ne passeront plus sur ta terre, encouragés par ta décrépitude. Tout est fini pour eux, ils ont été retranchés.
Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.

< Nahum 1 >