< Michée 6 >

1 Écoutez donc la parole: Le Seigneur, le Seigneur a dit: Lève-toi, annonce le jugement aux montagnes, et que les collines entendent ta voix!
Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
2 Écoutez, montagnes, le jugement du Seigneur, et vous aussi, vallées, fondements de la terre; car le Seigneur vient en jugement devant Son peuple, et Il plaidera avec Israël.
Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
3 Mon peuple, que t'ai-Je fait? En quoi t'ai-Je contristé? En qui t'ai-Je déplu? Réponds-Moi.
“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
4 Est-ce parce que Je t'ai fait sortir de la terre d'Égypte, que Je t'ai affranchi de la maison de servitude, et que J'ai envoyé devant toi Moïse, Aaron et Marie?
Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
5 Mon peuple, souviens-toi donc de ce qu'a médité contre toi Balac, roi de Moab, et de la réponse que lui a rapportée Balaam, fils de Béor, depuis Sétim jusqu'à Galgala, afin que l'on connût la justice du Seigneur.
Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
6 Comment prendrai-je le Seigneur? Comment serai-je agréable à mon Dieu très-haut? Le prendrai-je par des holocaustes, par des veaux d'un an?
Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
7 Le Seigneur accueillera-t-Il des milliers de béliers, des myriades de chèvres grasses? Donnerai-je, pour mes impiétés, les premiers-nés de mes troupeaux, et, pour les péchés de mon âme, le fruit de mes entrailles?
Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
8 Ô homme, faut-il te dire ce qui est bon? Est-ce que le Seigneur demande de toi quelque chose, sinon que tu pratiques la justice, que tu aimes la miséricorde, et que tu sois prêt à cheminer avec le Seigneur ton Dieu?
Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
9 La voix du Seigneur sera invoquée dans la ville, et sauvera ceux qui craignent Son Nom. Écoute, tribu: Qui donc mettra l'ordre en ta cité?
Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
10 Est-ce le feu? Est-ce la maison de l'impie amassant des trésors iniques, avec une insolente impiété?
Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
11 Sera-t-il absous, l'homme injuste avec ses fausses balances et ses faux poids en un sac?
Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
12 Car c'est ainsi que ceux qui demeurent dans la ville ont amassé leurs richesses impies; et ils ne disent que des mensonges, et dans leur bouche leur langue s'est enorgueillie.
Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
13 Et Moi Je commencerai par te frapper, et Je t'effacerai à cause de tes crimes.
Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
14 Tu mangeras, et ne seras point rassasié, et il y aura sur toi des ténèbres; et le Seigneur Se détournera; tu ne seras point sauvée; et ceux qui échapperont seront livrés au glaive.
Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
15 Tu sèmeras et ne moissonneras pas; tu pressureras l'olive, et tu ne seras pas oint de son huile; tu pressureras la grappe, et tu n'en boiras pas le vin; et les lois de Mon peuple seront abolies.
Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
16 Car tu as gardé les ordonnances de Zambri, et toutes les œuvres de la maison d'Achab; et tu as marché dans toutes leurs voies, pour que Je te livre, toi, à la destruction et aux sifflets de tes habitants; et vous recueillerez les opprobres des peuples.
Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”

< Michée 6 >