< Malachie 2 >
1 Et maintenant voici un ordre pour vous, ô prêtres
“Tsono chenjezo ili ndi la inu, inu ansembe.”
2 Si vous Me désobéissez, et si vous ne mettez pas en vos cœurs qu'il faut glorifier Mon Nom, dit le Seigneur tout-puissant, Je vous enverrai Ma malédiction; et votre bénédiction sera maudite, et Je la maudirai, et Je la rendrai vaine, et la Mienne ne sera pas en vous, parce que vous n'aurez point déposé Mes paroles en vos cœurs.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati simumvera, ndipo ngati simulemekeza dzina langa mʼmitima mwanu, ndidzakutembererani ndipo madalitso onse munawalandira ndidzawatemberera. Ndithu, ndawatemberera kale, chifukwa simunalemekeze Ine mʼmitima mwanu.”
3 Voilà que Je vous prive de l'épaule de vos victimes, et Je répandrai sur votre face leur fiente, la fiente de vos fêtes, et Je vous prendrai en même temps à leur place.
“Ine ndidzalanga zidzukulu zanu chifukwa cha inu; ndidzakupakani kumaso ndowe za nsembe zanu zachikondwerero, ndipo ndidzakutayani pamodzi ndi ndowezo.”
4 Et vous connaîtrez que c'est Moi qui vous ai envoyé ce commandement, que Mon alliance doit être avec les lévites, dit le Seigneur tout-puissant.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Apo mudzadziwa kuti Ine ndatumiza chenjezoli kuti pangano langa ndi Levi lipitirire.
5 Mon alliance était avec Lévi, une alliance de vie et de paix, et Je lui avais donné Ma crainte, de sorte qu'à Mon Nom il était frappé de crainte.
Ine ndinali naye pa pangano, pangano lopatsa moyo ndi mtendere, ndipo ndinamupatsa zimenezi kuti azindiopa, ndipo anandiopadi ndi kulemekeza dzina langa.
6 La loi de vérité était en sa bouche, et nulle iniquité n'eût été trouvée sur ses lèvres; il marchait avec Moi, dirigeant sa voie en paix, et il a détourné du mal nombre d'hommes.
Pakamwa pake pankatuluka malangizo woona, ndipo pa milomo yake sipanapezeke chinyengo. Iye anayenda nane mwamtendere ndi molungama mtima, ndipo anabweza anthu ambiri mʼnjira zawo zauchimo.
7 Les lèvres du prêtre doivent garder la doctrine; on cherchera la loi dans les paroles de sa bouche; car il est l'envoyé du Seigneur tout-puissant.
“Pakuti wansembe ayenera kukhala ndi chidziwitso, ndipo anthu ayenera kufunafuna malangizo kuchokera kwa iye, popeza iye ndi mthenga wa Yehova Wamphamvuzonse.
8 Mais vous vous êtes retirés de la voie, et vous avez détourné plusieurs de la loi, et vous avez profané l'alliance de Lévi, dit le Seigneur tout-puissant.
Koma inu mwasiya njira yanga ndipo mwapunthwitsa anthu ambiri ndi ziphunzitso zanu; mwayipitsa pangano langa ndi Levi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
9 Aussi ai-Je fait de vous le mépris et le rebut de toutes les nations, parce que vous n'avez point gardé Mes voies, mais qu'en la loi vous avez fait acception des personnes.
“Choncho Ine ndachititsa kuti munyozedwe ndi kuchititsidwa manyazi pamaso pa anthu onse, chifukwa simunatsate njira zanga koma mwakhala mukuonetsa kukondera pa nkhani za malamulo.”
10 N'avez-vous pas tous un seul Père? N'est-ce pas le Dieu unique qui vous a créés? Pourquoi donc chacun de vous a-t-il abandonné son frère en souillant l'alliance de vos ancêtres?
Kodi sitili naye Atate mmodzi tonsefe? Kodi anatilenga si Mulungu mmodzi? Chifukwa chiyani tikudetsa pangano la makolo athu posamakhulupirirana wina ndi mnzake?
11 Juda a failli, et l'abomination a été en Israël et en Jérusalem, parce que Juda a profané les choses saintes du Seigneur, où Dieu Se complaisait, et qu'il s'est attaché à des dieux étrangers.
Yuda waleka kukhulupirika. Chinthu chonyansa chachitika mu Israeli ndi mu Yerusalemu: Yuda wayipitsa malo opatulika amene Yehova amawakonda, pokwatira mkazi wopembedza mulungu wachilendo.
12 Le Seigneur exterminera tout homme qui fera ainsi pour l'expulser des tentes de Jacob, et le séparer de ceux qui sacrifient au Seigneur tout- puissant.
Ndipo wina aliyense wochita zimenezi, kaya munthuyo ndi wotani, Yehova amuchotse ku banja la Yakobo, ngakhale atabweretsa zopereka kwa Yehova Wamphamvuzonse.
13 Et vous avez fait ce que Je déteste; vous avez couvert de larmes l'autel du Seigneur: vous vous êtes frappé la poitrine au milieu des cris et des gémissements. Est-il convenable que Je considère vos victimes, ou que J'agrée quelque chose de vos mains?
China chimene mumachita ndi ichi: Mumakhathamiritsa guwa lansembe la Yehova ndi misozi. Mumalira ndi kufuwula kwambiri chifukwa Iye amakana kuyangʼana nsembe zanu, kapena kulandira mokondwera nsembe za mʼmanja mwanu.
14 Et vous avez dit: Pour quel motif? C'est parce que le Seigneur a porté témoignage contre toi et la femme de ta jeunesse que tu as abandonnée: elle qui était ta compagne; elle qui était la femme de ton alliance.
Inu mukufunsa kuti, “Chifukwa chake nʼchiyani?” Chifukwa chake nʼchakuti Yehova ndi mboni ya pangano limene unachita ndi mkazi wa unyamata wako, chifukwa sunakhulupirike kwa iye, ngakhale kuti iyeyo ndiye mnzako, ndi mkazi wako mwapangano.
15 Ne l'a-t-Il pas éternellement créée? n'est-elle pas Son esprit? Et tu as dit: Que demande Dieu, sinon des enfants issus de moi? Or garde cette parole en ton esprit: N'abandonne pas la femme de ta jeunesse.
Kodi Yehova sanawalenge iwo ngati munthu mmodzi? Ndi ake mʼthupi ndi mu mzimu. Nʼchifukwa chiyani ali mmodzi? Chifukwa Iye amafuna ana opembedza Mulungu. Motero samala moyo wako wauzimu, ndipo usakhale wosakhulupirika kwa mkazi wa unyamata wako.
16 Mais si, l'ayant haïe, tu la répudies, dit le Seigneur Dieu d'Israël, l'impiété couvrira toutes tes pensées, dit le Seigneur tout-puissant; c'est pourquoi garde cette parole en ton esprit: N'abandonne pas la femme de ta jeunesse.
Yehova Mulungu wa Israeli akuti, “Ndimadana ndi kulekana ukwati. Ndimadana ndi munthu wochita zankhanza zotere kwa mkazi wake,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Choncho tetezani mzimu wanu, ndipo musakhale osakhulupirika.
17 Ô vous qui, par vos paroles, provoquez Dieu, et qui dites: En quoi L'avons-nous provoqué? C'est en disant: Quiconque fait le mal est bien vu du Seigneur; Il Se complaît en ceux-là; où donc est le Dieu de la justice?
Mwamutopetsa Yehova ndi zoyankhula zanu. Inu mukufunsa kuti, “Kodi tamutopetsa bwanji?” Mwamutopetsa ponena kuti, “Aliyense amene amachita zoyipa ndi wabwino pamaso pa Yehova ndipo iye amakondwera naye” kapena pofunsa kuti, “Ali kuti Mulungu woweruza mwachilungamo?”