< Lévitique 14 >

1 Et le Seigneur parla à Moïse, disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Voici la loi du lépreux: le jour où il sera purifié on le conduira au prêtre;
“Malamulo a munthu wakhate pa tsiku la kuyeretsedwa kwake ndi awa: Abwere naye kwa wansembe.
3 Celui-ci sortira du camp et l'inspectera; s'il voit que la tache de lèpre est guérie sur le lépreux,
Wansembe atuluke kunja kwa msasa ndipo amuonetsetse wodwalayo. Ngati munthu wakhateyo wachira,
4 Il donnera ses ordres, et l'on prendra pour le purifier deux petits oiseaux purs et vivants, ainsi que du bois de cèdre, de l'écarlate filé et de l'hysope.
wansembe alamule anthu kuti amutengere wodwala woti ayeretsedweyo, mbalame zamoyo ziwiri zomwe Ayuda amaloledwa kudya, nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope.
5 Le prêtre donnera ses ordres, et l'on égorgera l'un des oiseaux, dans un vase de terre, sur de l'eau vive.
Wansembe alamule anthuwo kuti mbalame imodzi ayiphere mu mʼphika wa dothi pamwamba pa madzi abwino.
6 Le prêtre prendra l'oiseau vivant, avec le bois de cèdre, l'écarlate filé et l'hysope, et il les trempera dans le sang de l'oiseau égorgé sur de l'eau vive.
Kenaka wansembe atenge mbalame yamoyo ija ndi kuyinyika pamodzi ndi nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope kaja mʼmagazi ambalame imene anayiphera pamwamba pa madzi abwino.
7 Il aspergera sept fois le purifié, et celui-ci sera pur; puis il laissera l'oiseau vivant s'envoler dans la campagne.
Wansembe awaze magazi kasanu ndi kawiri pa munthu woti amuyeretse khateyo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa. Kenaka wansembe awulutsire ku thengo mbalame yamoyoyo.
8 Le purifié lavera ensuite ses vêtements, et on lui rasera tout le corps; on le lavera avec de l'eau, et il sera pur; après cela, il entrera dans le camp et demeurera sept jours hors de sa maison.
“Munthu amene wayeretsedwa uja achape zovala zake, amete tsitsi lake lonse, ndipo asambe mʼmadzi. Akatero adzakhala woyeretsedwa. Atatha zimenezi munthuyo apite ku msasa wake koma akhale kunja kwa msasawo kwa masiku asanu ndi awiri.
9 Le septième jour, on lui rasera la tête, le menton, les sourcils, et tout le corps; il lavera ses vêtements, et il se lavera le corps avec de l'eau, et il sera pur.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri amete tsitsi lake lonse: amete kumutu, ndevu zake, nsidze zake pamodzi ndi tsitsi lina lonse. Kenaka achape zovala zake ndi kusamba mʼmadzi, ndipo adzakhala woyeretsedwa.
10 Le huitième jour, il prendra deux agneaux d'un an sans tache, et une brebis d'un an sans tache, pour le sacrifice, ainsi que trois dixièmes d'éphi de fleur de farine pétrie dans l'huile, et une mesure d'huile.
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu munthuyo atenge ana ankhosa aamuna awiri ndi mwana wankhosa wamkazi wa chaka chimodzi. Zonsezi zikhale zopanda chilema. Atengenso chopereka chachakudya cha ufa wosalala wa makilogalamu atatu wosakaniza ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita.
11 Le prêtre qui purifiera l'homme, le placera avec les offrandes, en présence du Seigneur, devant la porte du tabernacle du témoignage.
Wansembe amene ati ayeretse munthu wodwalayo amuyimitse munthuyo ali ndi zopereka zake zonse pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
12 Puis, il prendra l'un des deux agneaux, et il l'offrira pour le délit, en même temps que la mesure d'huile, et il les mettra à part devant le Seigneur.
“Ndipo wansembe atenge mwana wankhosa wamwamuna mmodzi ndi kumupereka kuti akhale nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita. Wansembe aziweyule zonsezi pamaso pa Yehova kuti zikhale chopereka choweyula.
13 On égorgera l'agneau dans le lieu où l'on immole les holocaustes et les victimes pour le péché, dans le lieu saint. Car la victime pour le péché est comme celle pour le délit; elle appartient au prêtre, c'est chose très sainte.
Mwana wankhosayo amuphere pa malo amene amaphera nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yopsereza, kutanthauza malo opatulika. Monga zimakhalira ndi chopereka chopepesera machimo, chopereka ichi ndi chake cha wansembe ndipo ndi chopereka choyera kopambana.
14 Le prêtre prendra du sang de la victime pour le délit, et il en mettra sur l'oreille droite du purifié et sur l'extrémité de sa main droite, et sur l'extrémité de son pied droit.
Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera kupalamula ndi kuwapaka pa msonga pa khutu lakumanja la munthu woti ayeretsedweyo. Apakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndi chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
15 Ensuite le prêtre, ayant pris la mesure d'huile, en versera dans sa main gauche;
Wansembe atengeko mafuta pangʼono, nʼkuwathira mʼdzanja lake lamanzere,
16 Il trempera le doigt de la main droite dans l'huile de la main gauche, et il fera sept aspersions devant le Seigneur. Quant à l'huile restée dans sa main gauche,
aviyike chala chake cha ku dzanja lamanja mʼmafuta amene ali mʼdzanja lamanzerewo, ndi kuwaza mafutawo ndi chala chakecho kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
17 Il en mettra sur le lobe de l'oreille droite du purifié, et sur l'extrémité de sa main droite, et sur l'extrémité de son pied droit, comme il a mis du sang de la victime.
Wansembe apake mafuta otsala mʼdzanja lake pa khutu lakumanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Awapakenso pa chala chake chachikulu cha ku dzanja lamanja ndiponso pa chala chake chachikulu cha ku phazi lakumanja, pamalo pamene anali atapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula paja.
18 Puis, il répandra le reste de l'huile qu'il aura dans la main sur la tête du purifié, et il priera pour lui devant le Seigneur.
Mafuta onse otsala mʼdzanja la wansembe awathire pamutu pa munthu woti ayeretsedwe uja, ndipo potero adzachita mwambo womupepesera pamaso pa Yehova.
19 Après cela, le prêtre fera le sacrifice pour le péché, et il priera pour celui qui est purifié de son péché. Et le prêtre égorgera l'holocauste;
“Kenaka wansembe apereke nsembe yopepesera machimo kuti achite mwambo womupepesera munthu woti ayeretsedwe khate lake uja. Atatha kuchita zimenezi, wansembe aphe nyama ya nsembe yopsereza
20 Il portera l'holocauste et le sacrifice sur l'autel devant le Seigneur; et il priera pour l'homme, et celui-ci sera purifié.
ndi kuyipereka pa guwa, pamodzi ndi nsembe yachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera munthu wodzayeretsedwayo, ndipo adzakhala woyera.
21 Si l'homme est pauvre, si ses facultés sont insuffisantes pour qu'il apporte ces choses, il prendra comme offrande un seul agneau pour le délit, afin de se rendre Dieu propice, et il présentera un dixième d'éphi de fleur de farine pétrie dans l'huile, en sacrifice, et une mesure d'huile,
“Ngati munthu woti ayeretsedweyo ndi wosauka ndipo sangathe kupeza zinthu zimenezi, apereke mwana wankhosa wamwamuna monga nsembe yopepesera kupalamula ndipo ayiweyule pochita mwambo womupepesera. Aperekenso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala osakaniza ndi mafuta kuti ikhale nsembe yachakudya, pamodzi ndi mafuta wokwanira limodzi mwa magawo atatu a lita.
22 Et deux tourterelles ou deux petits de colombes, selon ce que lui permettront ses facultés, l'un pour le péché, l'autre pour l'holocauste.
Aperekenso njiwa ziwiri kapena mawunda awiri zomwe iye angathe kuzipeza. Imodzi ikhale nsembe yopepesera machimo, ndi inayo ikhale ya nsembe yopsereza.
23 Le huitième jour, pour être purifié, il portera ces offrandes au prêtre devant la porte du tabernacle du témoignage, en présence du Seigneur.
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu zonsezo abwere nazo kwa wansembe, pa khomo pa tenti ya msonkhano, pamaso pa Yehova kuti munthuyo ayeretsedwe.
24 Et le prêtre, ayant pris l'agneau du délit et la mesure d'huile, les placera, comme offrande, devant le Seigneur;
Wansembe atenge mwana wankhosa wopereka nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta aja, ndipo aziweyule kuti zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
25 Il égorgera l'agneau du délit, il prendra du sang de la victime et il en mettra sur le lobe de l'oreille droite du purifié, sur l'extrémité de sa main droite et sur l'extrémité de son pied droit.
Wansembe aphe nkhosa yopereka nsembe yopepesera kupalamula ndipo atenge magazi ake ndi kuwapaka pa msonga ya khutu lakumanja la munthu amene ayeretsedweyo. Awapakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndiponso pa chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
26 Ensuite, le prêtre se versera de l'huile dans la main gauche,
Kenaka wansembe athire mafuta mʼdzanja lake lamanzere,
27 Et avec le doigt de la main droite, il fera, devant le Seigneur, sept aspersions de l'huile de sa main gauche.
ndipo ndi chala chake cha ku dzanja lamanja awaze mafutawo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
28 Et le prêtre mettra de l'huile de sa main gauche sur le lobe de l'oreille droite du purifié, sur l'extrémité de sa main droite et sur l'extrémité de son pied droit, à la même place qu'il a mis le sang de la victime pour le délit.
Apakenso mafuta omwewo amene ali mʼdzanja lake lamanja pa msonga ya khutu la kudzanja lamanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Apakenso pa chala chachikulu cha phazi lakumanja, pamalo pamene anapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula.
29 Ce qui restera d'huile dans la main gauche du prêtre, il le répandra sur la tête du purifié, et le prêtre priera pour le purifié devant le Seigneur.
Mafuta onse otsala amene ali mʼdzanja la wansembe awapake pamutu pa munthu amene ayeretsedweyo kuti amuchitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.
30 Il sacrifiera les tourterelles ou jeunes colombes, selon ce que les facultés du purifié lui auront permis d'apporter,
Ndipo munthuyo apereke njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri, molingana ndi mmene anapezeramo,
31 L'une pour le péché, l'autre pour l'holocauste avec le sacrifice, et le prêtre priera pour le purifié devant le Seigneur.
imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza, pamodzi ndi chopereka chachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera machimo a munthu woti ayeretsedwe.
32 Telle est la règle pour la tache de lèpre et pour celui qui ne peut présenter toutes les offrandes de la purification.
“Amenewa ndi malamulo a munthu wakhate amene alibe zinthu zoti apereke pamene akuyeretsedwa.
33 Le Seigneur parla encore à Moïse et à Aaron, disant:
“Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
34 Lorsque vous serez entrés en la terre de Chanaan que je vous donne pour héritage, et que je ferai paraître la tache de lèpre sur les maisons de la terre qui vous appartiendra,
Mukakalowa mʼdziko la Kanaani limene ndikukupatsani kuti likhale lanu, ndipo Ine ndikakabweretsa ndere zoyanga mʼnyumba mʼdziko limenelo,
35 Le maître de la maison ira l'annoncer au prêtre, disant: Il se montre comme une tache dans ma maison.
mwini wake nyumbayo adzapite kwa wansembe ndi kukamuwuza kuti, ‘Ndaona chinthu chooneka ngati ndere mʼnyumba mwanga.’
36 Et le prêtre ordonnera que l'on démeuble la maison, avant qu'il y entre pour voir la tache, de peur que les meubles de la maison ne deviennent tous impurs; cela fait, il entrera pour visiter la maison.
Tsono wansembe alamule kuti anthu atulutse zinthu zonse mʼnyumbamo iye asanalowemo ndi kukaonetsetsa ndereyo kuti mʼnyumbamo musapezeke chinthu choti achitchule chodetsedwa. Izi zitachitika, wansembe alowe mʼnyumbamo ndi kukaonamo.
37 Puis, il observera la tache, et s'il voit des cavités verdâtres ou rousses qui s'enfoncent dans les murs,
Iye aonetsetse nderezo. Tsono akapeza kuti nderezo zili mʼkhoma la nyumba, ndipo ngati zili ndi mawanga obiriwira kapena ofiirira, komanso zikuoneka kuti zalowerera mpaka mʼkati mwa khoma,
38 Il sortira, et, se tenant sur la porte, il séparera la maison pendant sept jours.
wansembe atuluke mʼnyumbamo ndi kupita pa khomo, ndipo ayitseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri.
39 Le septième jour, le prêtre reviendra, et il examinera la maison, et s'il voit que la tache s'est étendue sur les murs,
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri wansembe abwerenso kudzayangʼana mʼnyumbamo. Ngati ndere yafalikira mʼmakoma a nyumbayo,
40 Il donnera ses ordres, et l'on enlèvera les pierres sur lesquelles est la tache, et on les jettera hors de la ville, en lieu impur;
wansembe alamule kuti anthu agumule miyala imene muli nderezo ndipo akayitaye kudzala la kunja kwa mzinda.
41 Ensuite, on raclera l'intérieur de la maison tout alentour, et la poussière enlevée sera jetée hors de la ville, en lieu impur;
Wansembe awuze anthu kuti apale makoma onse a mʼkati mwa nyumbayo, ndipo zopalidwazo akazitaye ku malo odetsedwa a kunja kwa mudzi.
42 On prendra d'autres pierres grattées que l'on mettra à la place de celles que l'on aura ôtées, et l'on prendra un autre enduit avec lequel la maison sera recrépie.
Tsono anthuwo atenge miyala ina ndi kuyilowetsa mʼmalo mwa miyala imene anagumula ija ndipo atenge dothi latsopano ndi kumata nyumbayo.
43 Si la tache revient dans la maison, après qu'on en aura enlevé les pierres, raclé et recrépi les murs,
“Ngati ndere iwonekanso mʼnyumbamo atagumula kale miyala ndiponso atayipala kale ndi kuyimatanso,
44 Le prêtre entrera encore et observera: si la tache s'est étendue dans la maison, c'est une lèpre persistante dans la maison; la maison est impure.
wansembe apite kukayionetsetsenso ndipo ngati nderezo zafalikira mʼnyumbamo, ndiye kuti ndere zimenezo ndi zoopsa. Nyumba imeneyo ndi yodetsedwa.
45 Alors, on démolira la maison, et l'on portera hors de la ville, en lieu impur, ses bois, ses pierres et tous les décombres.
Agwetse nyumbayo, ndipo miyala yake, matabwa pamodzi ndi dothi lake lonse, zonse akazitaye kudzala lodetsedwa, kunja kwa mzinda.
46 Celui qui sera entré dans la maison, durant l'un des jours où elle aura été séparée, sera impur jusqu'au soir.
“Aliyense amene alowa mʼnyumbamo itatsekedwa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
47 Celui qui aura couché dans la maison lavera ses vêtements et sera impur jusqu'au soir; celui enfin qui aura mangé dans la maison lavera ses vêtements et sera impur jusqu'au soir.
Munthu amene wagona mʼnyumbamo kapena kudyeramo ayenera kuchapa zovala zake.
48 Mais si le prêtre entre et examine, s'il voit que la tache ne s'est pas étendue dans la maison, après qu'on l'a recrépie, il purifiera la maison; la tache est effacée.
“Koma ngati pambuyo pa kuyimata, wansembe abwera kudzaonetsetsa mʼnyumbamo napeza kuti ndereyo sinafalikire, iye alengeze kuti nyumbayo ndi yoyeretsedwa, chifukwa ndereyo yatha.
49 Et il prendra, pour purifier la maison, deux oiseaux purs vivants, et du bois de cèdre, et de l'écarlate filé, et de l'hysope.
Kuti nyumbayo iyeretsedwe, mwini wake atenge mbalame ziwiri, kanthambi kamkungudza, kansalu kofiirira ndi kachitsamba ka hisope.
50 Il égorgera l'un des oiseaux, dans un vase de terre, sur de l'eau vive.
Wansembe aphe mbalame imodzi pamwamba pa madzi abwino mu mʼphika wa dothi.
51 Puis, il prendra le bois de cèdre, l'écarlate filé, l'hysope et l'oiseau vivant, et il les trempera dans le sang de l'oiseau égorgé sur de l'eau vive, et il fera dans la maison sept aspersions.
Kenaka atenge kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope, kansalu kofiirira pamodzi ndi mbalame yamoyo ija, zonsezi aziviyike mʼmagazi a mbalame yophedwa ija, ndiponso mʼmadzi abwino aja, ndipo awaze nyumbayo kasanu ndi kawiri
52 Il purifiera ainsi la maison par le sang de l'oiseau égorgé, et avec l'eau vive, l'oiseau vivant, le bois de cèdre, l'hysope et l'écarlate filé;
Akatero ndiye kuti wayeretsa nyumbayo ndi magazi a mbalame, madzi abwino, mbalame yamoyo, kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope ndi kansalu kofiirira.
53 Après quoi, il lâchera l'oiseau vivant hors de la ville dans la campagne; il priera pour la maison, et elle sera pure.
Kenaka ayiwulutsire mbalame yamoyo ija kuthengo, kunja kwa mzinda. Pamenepo ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera nyumbayo, ndipo idzakhala yoyeretsedwa.”
54 Telle est la loi pour toute tache de lèpre, toute plaie,
Amenewa ndiwo malamulo a nthenda ya khate, bala lonyerenyetsa,
55 Pour la lèpre de vêtements et de maisons,
nguwi za pa zovala, ndere za mʼnyumba,
56 Pour la lèpre provenant de cicatrices, de pustules et de taches luisantes;
khate la chithupsa, khate la mʼbuko ndi khate la banga
57 Et pour la notification du jour où l'on est impur et de celui où l'on est purifié: telle est la loi de la lèpre.
kuti mudziwe ngati chinthucho ndi choyeretsedwa kapena chodetsedwa. Amenewa ndiwo malamulo a nthenda zonse za khate.

< Lévitique 14 >