< Lamentations 4 >

1 Aleph. Comment l'or s'est-il terni? Comment l'argent pur s'est-il changé? Comment les pierres saintes ont-elles été dispersées aux coins de toutes les rues?
Haa! Golide wathimbirira, golide wosalala wasinthikiratu! Amwazamwaza miyala yokongola ya kumalo opatulika pamphambano ponse pa mzinda.
2 Beth. Les fils de Sion les plus honorés, ceux que l'on prisait autant que l'or, comment ont-ils été traités comme des vases de terre, œuvre des mains du potier?
Haa! Ana a Ziyoni amtengowapatali amene kale anali ngati golide, tsopano ali ngati miphika ya dothi, ntchito ya owumba mbiya!
3 Ghimel. Les dragons eux-mêmes ont découvert leurs mamelles; et leurs petits ont allaité les filles de mon peuple, pour leur communiquer leur incurable instinct, comme l'autruche dans le désert.
Ngakhale nkhandwe zimapereka bere kuyamwitsa ana ake, koma anthu anga asanduka ankhanza ngati nthiwatiwa mʼchipululu.
4 Daleth. La langue de l'enfant à la mamelle, s'est collée à son palais dans sa soif; les enfants ont demandé du pain, et nul n'était là pour leur en distribuer.
Lilime la mwana lakangamira kukhosi chifukwa cha ludzu, ana akupempha chakudya, koma palibe amene akuwapatsa.
5 Hé. Ceux qui se nourrissaient de mets délicats ont péri dans les rues; ceux qu'on avait élevés dans la pourpre ont été enfouis dans le fumier.
Iwo amene kale ankadya zonona akupemphetsa mʼmisewu ya mu mzinda. Iwo amene kale ankavala zokongola tsopano akugona pa phulusa.
6 Vav. L'iniquité de la fille de mon peuple a dépassé l'iniquité de Sodome, jadis renversée en un moment, sans que des hommes y aient fatigué leurs mains.
Kuyipa kwa anthu anga kunali kwakukulu kuposa anthu a ku Sodomu, amene anawonongedwa mʼkamphindi kochepa popanda owathandiza.
7 Zaïn. Les Nazaréens étaient plus blancs que la neige, plus éclatants que le lait; ils étaient comme purifiés par le feu; leur poli était supérieur à celui du saphir.
Akalonga ake anali owala koposa chisanu chowundana ndi oyera kuposa mkaka. Matupi awo anali ofiira kuposa miyala ya rubi, maonekedwe awo ngati miyala ya safiro.
8 Cheth. Et leur visage est devenu plus noir que la suie, on ne les reconnaît pas dans les rues; leur peau s'est collée sur leurs os; ils se sont desséchés comme du bois mort.
Koma tsopano maonekedwe awo ndi akuda kuposa mwaye; palibe angawazindikire mʼmisewu ya mu mzinda. Khungu lawo lachita makwinyamakwinya pa mafupa awo; lawuma gwaa ngati nkhuni.
9 Teth. Les hommes tués par le glaive étaient plus beaux que les hommes morts de faim; car ceux-ci s'en étaient allés transpercés par la disette des fruits de la terre.
Amene anaphedwa ndi lupanga aliko bwino kuposa amene anafa ndi njala; chifukwa chosowa chakudya cha mʼmunda iwowa ankafowoka ndi njala mpaka kufa.
10 Iod. Les mains des femmes, naturellement compatissantes, ont fait cuire leurs propres enfants; elles s'en sont nourries dans la ruine de la fille de mon peuple.
Amayi achifundo afika pophika ana awo enieni, ndiwo anali chakudya chawo pamene anthu anga anali kuwonongeka.
11 Caph. Le Seigneur a assouvi sa colère; il a répandu son indignation et ses fureurs, et il a allumé dans Sion un feu qui l'a dévorée jusqu'en ses fondements.
Yehova wakwaniritsa ukali wake; wagwetsa pansi mkwiyo wake woopsa. Ndipo wayatsa moto mʼZiyoni kuti uwononge maziko ake.
12 Lamed. Les rois de la terre, les peuples du monde entier ne croyaient pas qu'un ennemi, qu'un oppresseur pût entrer par les portes de Jérusalem.
Mafumu a pa dziko lapansi sanakhulupirire, kapena wina aliyense wokhala pa dziko lonse, kuti adani kapena ankhondo akhoza kulowa pa zipata za Yerusalemu.
13 Mem. À cause des péchés de ses prophètes, et des iniquités de ses prêtres, qui au milieu d'elle versaient le sang innocent,
Koma izi zinachitika chifukwa cha kuchimwa kwa aneneri ake ndi mphulupulu za ansembe ake, amene ankapha anthu osalakwa pakati pawo.
14 Noun. Les gardes ont chancelé dans les rues, ne pouvant éviter d'y marcher; ils se sont souillés de sang, et leurs robes y ont touché.
Tsopano akungoyendayenda mʼmisewu ya mu mzinda ngati anthu osaona. Iwo ndi odetsedwa kwambiri ndi magazi palibe yemwe angayerekeze nʼkukhudza komwe chovala chawo.
15 Samech. Éloignez-vous des impurs; criez-leur: Retirez-vous, retirez- vous, ne nous touchez pas; car ceux que les impurs ont touché ont chancelé; dites aux nations: Ils n'habiteront plus parmi nous.
Anthu akuwafuwulira kuti, “Chokani! Inu anthu odetsedwa!” “Chokani! Chokani! Musatikhudze ife!” Akamathawa ndi kumangoyendayenda, pakati pa anthu a mitundu yonse amati, “Asakhalenso ndi ife.”
16 Aïn. La présence du Seigneur était leur partage; il ne les considèrera plus; ils n'ont pas respecté le visage des prêtres; ils ont été sans miséricorde pour les prophètes.
Yehova mwini wake wawabalalitsa; Iye sakuwalabadiranso. Ansembe sakulandira ulemu, akuluakulu sakuwachitira chifundo.
17 Phé. Quand nous vivions encore, nos yeux se sont lassés à vainement regarder, et à attendre du secours.
Ndiponso maso athu atopa nʼkuyangʼana, chithandizo chosabwera nʼkomwe, kuchokera pa nsanja zathu tinadikirira mtundu wa anthu umene sukanatipulumutsa.
18 Tsadé. Nous nous sommes tournés vers une nation qui ne pouvait nous sauver; nous avons fait la chasse à nos petits enfants, de peur qu'ils ne sortissent dans les places publiques.
Anthu ankalondola mapazi athu, choncho sitikanayenda mʼmisewu yathu mu mzinda. Chimaliziro chathu chinali pafupi, masiku athu anali owerengeka, chifukwa chimaliziro chathu chinali chitafika.
19 Coph. Notre temps est proche; nos jours sont remplis; le moment est arrivé; nos persécuteurs sont venus, plus agiles que l'aigle dans le ciel; ils se sont élancés des montagnes; ils nous ont tendu des pièges dans le désert.
Otilondola akuthamanga kwambiri kuposa ziwombankhanga mu mlengalenga; anatithamangitsa mpaka ku mapiri ndi kutibisalira mʼchipululu.
20 Resch. L'esprit de notre face, le Christ Seigneur a été pris dans leurs filets, lui dont nous avons dit: Nous vivrons à son ombre parmi les nations!
Wodzozedwa wa Yehova, mpweya wathu wotipatsa moyo, anakodwa mʼmisampha yawo. Tinaganiza kuti tidzakhala pansi pa mthunzi wake pakati pa mitundu ya anthu.
21 Schin. Réjouis-toi, sois dans l'allégresse, fille de l'Idumée qui habite la terre; le calice du Seigneur passera aussi sur toi, tu t'enivreras, et tu vomiras ton ivresse.
Kondwera ndi kusangalala, mwana wamkazi wa Edomu. Iwe amene umakhala mʼdziko la Uzi. Koma iwenso chikho chidzakupeza; udzaledzera mpaka kukhala maliseche.
22 Thav. Ton iniquité a cessé, fille de Sion; ta captivité touche à son terme; mais le Seigneur a visité ton iniquité, fille d'Édom, et il a mis tes impiétés à découvert.
Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chako chidzatha; Iye sadzatalikitsa nthawi yako ya ukapolo. Koma Yehova adzalanga machimo ako, iwe mwana wamkazi wa Edomu, ndi kuyika poyera mphulupulu zako.

< Lamentations 4 >