< Lamentations 3 >

1 Aleph. Je suis l'homme qui voit sa misère, parce que la verge de la colère du Seigneur est sur moi.
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 Il m'a saisi et il m'a conduit dans les ténèbres, et non à la lumière.
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 Il n'a fait que tourner la main sur moi, durant tout le jour.
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 Il a envieilli ma peau et ma chair; il a brisé mes os.
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 Beth. Il a bâti contre moi; il a entouré ma tête; il a travaillé à ma perte;
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 Il m'a mis dans les ténèbres, comme les morts des siècles passés.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 Il a bâti contre moi, et je ne sortirai plus; il a appesanti mes fers.
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 Ghimel. Et quand je crierais, quand je l'invoquerais, c'est en vain; il a clos ma prière.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 Daleth. Il a muré mes voies; il a barricadé mes sentiers; il les a confondus.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 Il est pour moi une ourse qui me guette, un lion dans son repaire.
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 Il m'a poursuivi, comme je me détournais; il m'a arrêté, il m'a effacé;
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 Hé. Il a tendu son arc; il m'a fait tenir comme un but de flèches.
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 Il a plongé dans mes reins les traits de son carquois.
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 Je suis devenu la risée de tout mon peuple, le sujet de leurs chants, pendant tout le jour.
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 Vav. Il m'a nourri d'amertume; il m'a enivré de fiel.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 Il m'a brisé les dents avec des cailloux; il m'a donné à manger de la cendre.
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 Il a banni la paix de mon âme; j'ai oublié toutes mes joies:
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 Mes biens ont péri; mais mon espérance est dans le Seigneur.
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 Zaïn. Je me suis souvenu de ma misère; et, persécuté comme je suis, mon amertume et mon fiel
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 Ne seront pas oubliés; et les méditations de mon âme se tourneront contre moi.
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 Je les enfermerai dans mon cœur, et à cause de cela je souffrirai avec patience.
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 Teth. Le Seigneur est bon pour ceux qui l'attendent. C'est un bien pour l'âme de le chercher;
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 Teth. Le Seigneur est bon pour ceux qui l'attendent. C'est un bien pour l'âme de le chercher;
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 Teth. Le Seigneur est bon pour ceux qui l'attendent. C'est un bien pour l'âme de le chercher;
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 Teth. Le Seigneur est bon pour ceux qui l'attendent. C'est un bien pour l'âme de le chercher;
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 Elle patientera, elle attendra paisiblement le salut du Seigneur.
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 Il est bon à l'homme d'être soumis au joug dès sa jeunesse.
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 Il se tiendra solitaire; et il se taira, parce qu'il l'aura porté sur lui.
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 Iod. Il tendra la joue à qui le frappe; il se rassasiera d'opprobre,
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 Iod. Il tendra la joue à qui le frappe; il se rassasiera d'opprobre,
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 Parce que le Seigneur ne répudie pas pour toujours.
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 Coph. Si c'est lui qui a humilié, il aura compassion dans la plénitude de sa miséricorde.
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 Car ces paroles de colère ne sont pas selon son cœur, et ceux qu'il a abaissés sont des fils de l'homme.
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 Lamed. Mettre sous ses pieds tous les captifs de la terre,
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 Refuser justice à un homme devant le Très-Haut,
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 Condamner un homme quand on doit le juger, le Seigneur ne l'a pas dit.
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 Qui est celui qui a dit de telles choses, et a été obéi? Ce n'est pas le Seigneur qui les a commandées.
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 Le mal ne sortira pas de la bouche du Seigneur en même temps que le bien.
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 Mem. Pourquoi murmure-t-il, l'homme vivant, l'homme qui songe à son péché?
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 Noun. Votre voie a été examinée et recherchée, retournez au Seigneur.
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 Élevons nos cœurs sur nos mains, vers le Très-Haut, dans le ciel.
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 Nous avons péché, nous avons été impies, et vous ne nous avez point pardonné.
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 Samech. Vous avez gardé votre ressentiment, et vous nous avez poursuivis; vous avez tué, et vous n'avez rien épargné.
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 Vous vous êtes voilé d'une nuée pendant ma prière, pour ne plus me voir
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 Et pour me répudier; Aïn. Vous nous avez isolées au milieu des peuples.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 Tous nos ennemis ont ouvert la bouche contre nous.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 La crainte et la fureur, l'orgueil et la ruine sont venus en nous.
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 Mon œil répandra des torrents de larmes sur la destruction de la fille de mon peuple.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 Phé. Mon œil s'est consumé; et je ne me tairai point, parce qu'il n'y aura point de repos pour moi
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 Avant que le Seigneur, du haut des cieux, se penche et regarde.
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 Mon œil ravagera mon âme, à la vue de toutes les filles de la cité.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 Tsadé. Des oiseleurs m'ont fait la chasse comme à un passereau; ce sont tous ceux qui me haïssent sans raison.
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 Ils m'ont jeté dans une citerne pour m'ôter la vie, et ils en ont posé le couvercle sur moi.
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 L'eau s'est répandue sur ma tête, et j'ai dit: Je suis perdu.
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 Coph. J'ai invoqué votre nom, ô Seigneur, du fond de la citerne;
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 Vous avez entendu ma voix, et vous n'avez point fermé les oreilles à ma prière.
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 Vous êtes venu à mon secours le jour où je vous avais invoqué, et vous m'avez dit: Ne crains pas.
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 Resch. Seigneur, vous avez plaidé la cause de mon âme; vous avez racheté ma vie.
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 Seigneur, vous avez vu mes troubles; vous m'avez rendu justice.
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 Vous avez vu toute leur vengeance, tous leurs desseins sur moi.
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 Schin. Vous avez entendu leurs outrages, et tous leurs desseins contre moi,
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 Et les lèvres de mes oppresseurs, et leurs complots tramés contre moi tout le jour.
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 Soit qu'ils s'asseyent, soit qu'ils se lèvent, considérez leurs yeux.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 Seigneur, vous les rétribuerez selon les œuvres de leurs mains.
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 Thav. Vous leur ferez expier votre protection et les peines de mon cœur.
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 Vous les poursuivrez en votre colère, et vous les ferez disparaître de dessous le ciel, ô Seigneur.
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.

< Lamentations 3 >