< Juges 5 >
1 Ce jour-là, Débora et Barac, fils d'Abinéem, chantèrent ainsi:
“Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:
2 Une révélation s'est faite en Israël, quand le peuple a été de bonne volonté; bénissez le Seigneur.
“Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli; ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu, tamandani Yehova:
3 Ecoutez, rois; prêtez l'oreille, princes; je vais chanter un psaume au Seigneur Dieu d'Israël.
“Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu! Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova, Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.
4 Seigneur, quand vous êtes sorti de Séir, quand vous avez quitté les champs d'Edom, la terre a tremblé, le ciel a fait tomber de la rosée, les nuages ont répandu de l'eau.
“Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri, pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu, dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka nigwetsa madzi.
5 Les montagnes ont été ébranlées à la face du Seigneur Eloï, et aussi le Sina, à la face du Seigneur Dieu d'Israël.
Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova, Mulungu wa Israeli.
6 Durant les jours de Samegar, fils d'Anath, durant les jours de Jaël, ils ont quitté les voies, ils ont pris des sentiers, ils ont suivi des chemins détournés.
“Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati, pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa; alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.
7 Les hommes forts ont manqué en Israël, ils ont manqué jusqu'à ce que vint Débora, jusqu'à ce que s'élevât une mère en Israël.
Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi mpaka pamene iwe Debora unafika; unafika ngati mayi ku Israeli.
8 Ils s'étaient choisi de nouveaux dieux; alors, les ennemis ont attaqué même les villes des princes. Si l'on avait vu alors un bouclier et une lance parmi les quarante mille guerriers d'Israël!
Pamene anasankha milungu ina, nkhondo inabwera ku zipata za mzinda, ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.
9 Mon cœur est tout aux commandements donnés à Israël; vous qui parmi le peuple êtes de bonne volonté, bénissez le Seigneur.
Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli, uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu. Tamandani Yehova!
10 Vous qui montez sur des ânesses belles et luisantes, vous qui êtes assis sur le siège où l'on rend la justice, vous qui vous avancez sur la route des sièges ou vers cette route; racontez ces hauts faits,
“Inu okwera pa abulu oyera, okhala pa zishalo, ndi inu oyenda pa msewu, yankhulani.
11 Loin du bruit des perturbateurs, au milieu de ceux qui puisent paisiblement de l'eau, au lieu où l'on rend la justice. Seigneur, multipliez la justice en Israël. Alors, le peuple du Seigneur descendra aux portes de la ville.
Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta; kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana; akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli. “Choncho anthu a Yehova anasonkhana ku zipata za mzinda.
12 Réveille-toi, réveille-toi, Débora, réveille-toi, réveille-toi; chante un cantique; debout, ô Barac; emmène en captivité tes prisonniers, fils d'Abinéem.
Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera; tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo. Iwe Baraki! nyamuka Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’
13 Ce jour-là, est descendu ce qui restait des forts. Le peuple du Seigneur est descendu avec le Seigneur, et les vaillants excités par moi.
“Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo; anthu a Yehova anapita kukamenyera Yehova nkhondo kulimbana ndi adani amphamvu.
14 Ephraïm les a déracinés en Amalec, et, à votre suite, Seigneur, Benjamin et tout votre peuple. Ceux de Machir sont descendus avec moi, ardents à chercher l'ennemi; et ceux de Zabulon, même ceux qui maniaient la plume des scribes raconteurs.
Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu; akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako. Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri, ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.
15 Les princes d'Issachar étaient avec Débora; ainsi, elle envoya Balac à pied dans les vallons, sur le territoire de Ruben, où il y a grandes angoisses atteignant le cœur.
Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora; inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki, ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira. Koma pakati pa mafuko a Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.
16 Pourquoi demeurent-ils, au milieu des parcs, à entendre les beuglements de leurs grands troupeaux, pendant les discordes de Ruben? là, il y a de grandes épreuves du cœur.
Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera zitoliro zoyitanira nkhosa? Pakati pa anthu a fuko la Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.
17 Galaad est de l'autre côté du Jourdain, ou il a dressé ses tentes. Et Dan, pourquoi se tient-il sur ses barques? Aser s'est assis sur la côte maritime, il habite vers les embouchures de ses cours d'eau.
Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani. Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi? Aseri anali pa gombe la Nyanja; anangokhala mʼmadooko mwawo.
18 Le peuple de Zabulon a exposé sa vie à la mort; Nephthali est venu sur les hauts lieux de sa terre.
Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa. Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.
19 Les rois se sont ranges en bataille, les rois de Chanaan ont combattu en Thanaach, près des eaux de Mageddo; ils n'ont point recueilli de butin.
“Mafumu anabwera, anachita nkhondo; mafumu Akanaani anachita nkhondo ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido, koma sanatengeko zofunkha zasiliva.
20 Les étoiles, du haut du ciel, ont pris part à la lutte, sans quitter leurs voies; elles ont combattu contre Sisara.
Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo, zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.
21 Le torrent de Cison les a balayés, le torrent des anciens, le torrent de Cison! Mon âme dans sa force foulera aux pieds les ennemis.
Mtsinje wa Kisoni unawakokolola, chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola. Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!
22 Lorsque les jambes des chevaux furent embarrassées, ses forts se hâtèrent de fuir.
Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu, akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.
23 Maudite soit Méroz, dit l'ange du Seigneur, maudissez-la. Maudits soient tous ceux qui l'habitent, parce qu'ils ne sont point venus au secours du Seigneur, parce qu'ils ne lui ont point envoyé leurs hommes vaillants.
Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’ ‘Tembererani nzika zake mwaukali, chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova, kulimbana ndi adani ake amphamvu.’
24 Bénie soit, parmi les femmes, Jaël, l'épouse d'Haber le Cinéen; que sous leurs tentes les femmes la bénissent.
“Akhale wodala kupambana akazi onse, Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni; inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.
25 Il avait demandé de l'eau; elle lui donna du lait dans une coupe; elle lui présenta le beurre que l'on offre aux grands;
Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka; anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.
26 Elle étendit sa main gauche vers le clou et sa main droite vers le marteau des travailleurs; elle en frappa Sisara, elle fit entrer le clou dans sa tête, et elle frappa encore, et elle poussa le clou au travers de sa tempe.
Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake, anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja. Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake, ndi kumubowola mu litsipa mwake.
27 Et il roula entre ses pieds, il défaillit, et il mourut entre ses pieds; il s'était étendu devant elle, et il mourut dans son sommeil, et, au lieu même ou il s'était endormi, la vie l'abandonna.
Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa, anagwa; iye anagona pamenepo. Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa; pamene anagwera, pamenepo anaferapo.
28 La mère de Sisara s'est penchée à sa fenêtre, et, regardant par le treillis, elle a dit: Pourquoi son char tarde-t-il? D'où vient que son attelage se fait attendre?
“Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera; nafuwula mokweza kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika? Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’
29 Les sages princesses qui l'entouraient lui ont répondu, et elle-même a répété leurs paroles:
Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha, ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,
30 Ne le trouvera-t-on pas distribuant le butin? Mais elle pleurera, et pleurera sur la tête de l'homme; des étoffes teintes pour Sisara, des étoffes teintes de couleurs diverses, de riches étoffes, des dépouilles, tout autour de sa tête!
‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane; akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri. Sisera akumupatsa zofunkha: zovala zonyikidwa mu utoto, zoti ndizivala mʼkhosi zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’
31 Ainsi périssent tous vos ennemis, ô Seigneur! Que ceux qui aiment le Seigneur soient comme le lever du soleil dans toute sa puissance. La terre ensuite fut en repos durant quarante années.
“Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke, koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa pamene lituluka ndi mphamvu zake.” Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.