< Juges 4 >
1 Mais, les fils d'Israël recommencèrent à faire le mal devant le Seigneur, et Aod était mort.
Ehudi atamwalira, Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova.
2 Le Seigneur alors livra les fils d'Israël aux mains de Jabin, roi de Chanaan, qui régnait en Asor; le général de son armée était Sisara, et celui- ci demeurait en Arisoth des gentils.
Choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Yabini, mfumu ya ku Kanaani, imene inkalamulira ku Hazori. Mkulu wa ankhondo ake anali Sisera, amene ankakhala ku Haroseti-Hagoyimu.
3 Et les fils d'Israël crièrent au Seigneur, parce que ce roi avait neuf cents chars armés de faux, et que depuis vingt ans il opprimait cruellement Israël.
Aisraeli analira kwa Yehova kuti awathandize, chifukwa Sisera anali ndi magaleta achitsulo 900 ndipo anazunza Aisraeli mwankhanza kwa zaka makumi awiri.
4 En ce temps-là, Débora, prophétesse, femme de Lapidoth, jugeait Israël.
Debora, mneneri wamkazi, mkazi wake wa Rapidoti ndiye ankatsogolera Israeli nthawi imeneyo.
5 Elle siégeait sous le palmier de Débora, entre Rhama et Béthel, dans les montagnes d'Ephraïm; et les fils d'Israël venaient à elle pour être jugés.
Iye ankakhala pansi pa mtengo wa mgwalangwa wa Debora, pakati pa Rama ndi Beteli mʼdziko la ku mapiri la Efereimu, ndipo Aisraeli ankapita kwa iye kuti akaweruze milandu yawo.
6 Débora envoya chercher Barac, fils d'Abinéem, de Cadès en Nephthali, et elle lui dit: Le Seigneur ne t'a-t-il pas donné ces ordres: Tu t'en iras au mont Thabor; tu prendras avec toi dix mille hommes des fils de Nephthali et des fils de Zabulon, puis,
Debora uja anatuma munthu kuti akayitane Baraki mwana wa Abinoamu wa ku Kedesi mʼdziko la Nafutali ndipo anati kwa iye, “Yehova Mulungu wa Israeli akukulamula iwe kuti, ‘Pita kasonkhanitse anthu ku phiri la Tabori. Ubwere nawo anthu 10,000 a fuko la Nafutali ndi a fuko la Zebuloni.
7 J'amènerai vers toi, dans le torrent de Cison, Sisara, général de l'armée de Jabin, et ses chars, et ses troupes, et je le livrerai à tes mains?
Ine ndidzakokera Sisera mkulu wa ankhondo a Yabini pamodzi ndi magaleta ake ndi asilikali ake kwa inu ku mtsinje wa Kisoni ndipo ndidzamupereka mʼmanja mwanu.’”
8 A quoi Barac répondit: Si tu pars avec moi, je partirai; sinon, je ne partirai pas: car je ne sais pas le jour où le Seigneur me favorisera de la compagnie de son ange.
Baraki anamuyankha kuti, “Mukapita nane limodzi ine ndipita. Koma ngati sitipitira limodzi, inenso sindipita.”
9 Et elle dit: Je partirai avec toi; mais sache que tu n'auras point le premier rang dans la voie où tu veux marcher; car le Seigneur livrera Sisara aux mains d'une femme. Débora se leva donc, et elle partit de Cadès avec Barac.
Debora anati, “Chabwino, ine ndipita nawe limodzi. Koma mudziwe kuti inu simudzalandirapo ulemu pa zimene mwachitazi popeza Yehova wapereka Sisera mʼmanja mwa munthu wamkazi.” Choncho Debora ananyamuka kupita ku Kedesi pamodzi ndi Baraki.
10 Et Barac appela de Cadès le secours de Zabulon et de Nephthali; dix mille hommes le suivirent, et Débora partit avec lui.
Baraki anayitana mafuko a Zebuloni ndi Nafutali kuti abwere ku Kedesi. Anthu 10,000 anamutsatira, ndipo Debora anapita naye pamodzi.
11 Or, Haber le Cinéen s'était éloigné de Caina et des fils de Jobab, allié de Moïse; et il avait dressé sa tente vers le Chêne des Ravisseurs, qui touche à Cadès.
Nthawi imeneyo nʼkuti Mkeni wina dzina lake Heberi atalekana ndi Akeni anzake, zidzukulu za Hobabu, mlamu wa Mose, nakamanga tenti yake pafupi ndi mtengo wa thundu ku Zananimu pafupi ndi Kedesi.
12 Quand on apprit à Sisara que Barac, fils d'Abinéem, était allé sur le mont Thabor,
Pamene Sisera anamva kuti Baraki mwana wa Abinoamu wapita ku phiri la Tabori,
13 Sisara rassembla tous ses chars, ses neuf cents chars armés de faux, avec tout le peuple qui habitait comme lui Arisoth des gentils, et il les mena dans le torrent de Cison.
anasonkhanitsa magaleta ake achitsulo 900 ndi anthu onse amene anali naye ndipo anachoka ku Haroseti-Hagoyimu kupita ku mtsinje wa Kisoni.
14 Débora dit à Barac: Debout, voici le jour où le Seigneur te livre Sisara; car le Seigneur va marcher à notre tête. Et Barac descendit du mont Thabor suivi de dix mille hommes.
Debora anawuza Baraki kuti, “Dzukani! Paja ndi lero limene Yehova wapereka Sisera mʼmanja mwako. Kodi Yehova sanakhale akukutsogolerani?” Choncho Baraki anatsika phiri la Tabori, anthu 10,000 akumutsata.
15 Et le Seigneur frappa Sisara d'épouvante; ses chars s'embarrassèrent; tout son camp fut passé au fil de l'épée devant Barac; et Sisara descendit de son char, et il s'enfuit à pied.
Yehova anasokoneza Sisera ndi magaleta ake pamodzi ndi ankhondo ake onse. Baraki ndi anthu ake anawapirikitsa ndipo Sisera anatsika pa galeta yake nayamba kuthawa pansi.
16 Et Barac poursuivit ses chars et les débris du camp jusqu'à Arisoth des gentils; toute l'armée de Sisara fut passée au fil de l'épée; il n'en resta pas un seul homme.
Baraki analondola magaletawo pamodzi ndi ankhondo onse mpaka ku Haroseti-Hagoyimu, ndipo ankhondo onse a Sisera anaphedwa ndi lupanga. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe anatsala.
17 Cependant, Sisara s'enfuit à pied dans la tente de Jaël, femme du Cinéen Haber son ami; car il y avait paix entre Jabin, roi d'Asor, et Haber le Cinéen.
Komabe Sisera anathawa pansi mpaka anakafika ku tenti ya Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni uja, chifukwa panali mtendere pakati pa Yabini mfumu ya Hazori ndi banja la Heberi, Mkeni uja.
18 Et Jaël sortit à la rencontre de Sisara, et elle lui dit: Entre, mon seigneur, cache-toi chez moi, n'aie point de crainte. Et il se cacha chez elle dans la tente, et elle l'enveloppa d'un manteau.
Yaeli anatuluka kukachingamira Sisera ndipo anati, “Bwerani mbuye wanga, lowani momwemo musaope.” Choncho analowa mʼtenti muja, ndipo anamufunditsa chofunda.
19 Or, Sisara lui dit: Donne-moi à boire un peu d'eau, car j'ai bien soif. Et elle lui ouvrit l'outre à lait, et elle le fit boire; puis, elle le recouvrit.
Anati, “Ndili ndi ludzu, chonde patseniko madzi pangʼono akumwa, ndili ndi ludzu.” Mkaziyo anatsekula thumba la chikopa mmene munali mkaka, namupatsa kuti amwe, ndipo anamufunditsanso.
20 Et Sisara lui dit: Tiens-toi devant la porte de la tente; et si quelqu'un vient à toi, et te demande: Y a-t-il ici un homme? Réponds: Il n'y en a point.
Kenaka anawuza mkaziyo kuti, “Muyime pa khomo la tentili, ndipo munthu wina akabwera kudzakufunsani kuti, ‘Kodi kwafika munthu wina kuno?’ Inu muyankha kuti, ‘Ayi.’”
21 Et Jaël, femme d'Haber, prit un des clous de la tente; elle mit un marteau dans sa main, elle s'approcha de Sisara furtivement, et elle lui enfonça dans la tempe le clou qui traversa de part en part jusqu'à terre; et l'homme, perdant connaissance, fut enveloppe de ténèbres, et il mourut.
Koma Yaeli mkazi wa Heberi, anatenga chikhomo cha tenti ndi hamara ndi kupita mwakachetechete kwa Sisera uja. Tsono Sisera ali mtulo chifukwa chotopa, mkazi uja anamukhomera chikhomo chija mʼmutu mwake. Chinatulukira kwinaku mpaka kulowa mʼnthaka, ndipo anafa pomwepo.
22 Bientôt Barac parut poursuivant Sisara; Jaël sortit à sa rencontre, et elle lui dit: Viens, je vais te montrer l'homme que tu cherches. Il entra auprès d'elle, et il vit Sisara étendu mort, le clou dans la tempe.
Baraki atafika akulondola Sisera, Yaeli anatuluka kukamuchingamira namuwuza kuti, “Lowani mudzaone munthu amene mukumufunafuna.” Tsono atalowa anangoona Sisera ali thapsa pansi wakufa ndi chikhomo chili mʼmutu mwake.
23 Ainsi, le Seigneur Dieu, ce jour-là, mit en déroute le roi Jabin, devant les fils d'Israël.
“Choncho pa tsiku limenelo Mulungu anagonjetsa Yabini mfumu ya Akanaani, pamaso pa Aisraeli.
24 Et la main des fils d'Israël prévalut de plus en plus contre Jabin, roi de Chanaan, jusqu'à ce qu'ils l'eussent détruit.
Ndipo Aisraeli anapanikizabe Yabini, mfumu ya Akanaani, mpaka kumuwonongeratu.