< Juges 16 >

1 Et Samson alla a Gaza, où il vit une femme prostituée, chez laquelle il entra.
Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake.
2 Des gens l'apprirent aux hommes de Gaza, disant: Samson est venu ici. Et ils l'entourèrent, et ils l'épièrent à la porte de la ville, et ils ne bougèrent de toute la nuit, disant: Quand l'aurore brillera, nous le tuerons.
Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”
3 Samson resta couché jusqu'à minuit, et, s'étant levé au milieu de la nuit, il prit les portes de la ville avec les deux jambages; puis, les soulevant à l'aide du verrou, il les mit sur ses épaules. Alors, il monta au sommet de la montagne qui fait face à Hébron, où il les déposa.
Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.
4 Après cela, il aima une femme d'Alsorech, dont le nom était Dalila.
Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila.
5 Et les chefs des Philistins allèrent trouver cette femme, et ils lui dirent: Trompe-le; découvre en quoi réside sa grande force, et comment nous prévaudrons sur lui; puis, nous l'enchaînerons afin de l'humilier. Et nous te donnerons chacun onze cents sicles d'argent.
Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”
6 Dalila dit donc à Samson: Fais-moi connaître en quoi réside ta grande force, et comment tu pourrais être enchaîné et vaincu.
Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”
7 Samson lui dit: Si l'on m'attachait avec sept cordes humides, nullement altérées, je serais énervé, et je ressemblerais à un autre homme.
Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”
8 Les chefs des Philistins lui apportèrent sept cordes humides, nullement altérées; et, avec ces cordes, elle l'attacha.
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni.
9 Et ils se tenaient cachés dans sa chambre, et elle lui dit: Voici les Philistins, Samson. Et il rompit les cordes comme on brise une tresse d'étoupes, des qu'on lui fait sentir le feu; et la cause de sa force resta inconnue.
Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.
10 Et Dalila dit à Samson: Voilà que tu m'as trompée en me disant des mensonges. Apprends-moi, maintenant, avec quels liens il faudrait t'enchaîner?
Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”
11 Et il lui dit: Si l'on me liait de cordes neuves, avec lesquelles on n'ait encore fait aucune œuvre, je serais énervé et je ressemblerais à un autre homme.
Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”
12 Et Dalila prit des cordes neuves, et, avec ces cordes, elle l'attacha. Cependant, les chefs sortirent de leur cachette, et elle dit: Voici les Philistins, Samson. Il rompit les cordes autour de ses bras comme de l'étoupe.
Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.
13 Et Dalila dit à Samson: Voilà que tu m'as trompée en me disant des mensonges; apprends-moi avec quels liens il faudrait t'enchaîner. Et il lui répondit: Si tu faisais un tissu des sept tresses de ma tête et d'une chaîne de fil, si tu l'enfonçais dans le mur, en le maintenant par un clou, je serais aussi faible qu'un autre homme.
Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.” Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.”
14 Dès qu'il fut endormi, Dalila prit les sept tresses de sa tête; elle en fit un tissu avec une chaîne de fil, elle fixa ce tissu dans le mur à l'aide d'un clou, et elle dit: Voici les Philistins, Samson. Soudain, il sortit de son sommeil, et il arracha du mur le clou du tissu, et l'origine de sa force ne fut pas connue
Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo. Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.
15 Et Dalila dit à Samson: Comment dis-tu: Je t'aime, quand ton cœur n'est point avec moi? Tu m'as trois fois trompée, et tu ne m'as point appris en quoi réside ta grande force.
Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.”
16 Elle en vint donc à le poursuivre de ses paroles pendant des jours entiers, à le tourmenter, à affaisser son courage, jusqu'à le réduire à l'extrémité.
Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.
17 Et il lui ouvrit sans réserve son cœur, et il lui dit: Jamais le fer n'a passé sur ma tête, parce que, depuis les entrailles de ma mère, je suis consacré au Seigneur; lors donc qu'on me rasera, ma force s'évanouira; je serai énervé, et je ressemblerai à un autre homme.
Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”
18 Dalila vit bien qu'il lui avait ouvert son cœur sans réserve, et elle envoya chercher les chefs des Philistins, disant: Venez, cette fois encore, car il m'a ouvert son cœur sans réserve. Et les chefs des étrangers allèrent auprès d'elle, et ils apportèrent l'argent dans leurs mains.
Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo.
19 Et Dalila endormit Samson sur ses genoux; puis, elle appela un homme qui rasa les sept tresses de sa tête; et elle fut la première à l'humilier, car sa force s'était évanouie.
Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.
20 Dalila dit: Voici les Philistins, Samson. Et il s'éveilla, se disant: J'en sortirai comme les autres fois, et je saurai me délivrer; car il ignorait que le Seigneur s'était retiré de lui.
Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.
21 Mais les Philistins le saisirent, lui arrachèrent les yeux, et le transportèrent à Gaza, ou ils le mirent en prison avec des entraves d'airain aux pieds; enfin, ils lui firent tourner la meule, dans la maison du geôlier.
Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende.
22 Et sa chevelure commença à repousser après qu'il eut été rasé.
Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.
23 Et les chefs des Philistins étaient réunis pour offrir un grand sacrifice à Dagon leur dieu, et pour se réjouir, Dieu a livré, disaient-ils, à nos mains Samson notre ennemi.
Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”
24 Et le peuple l'a vu, et il a chanté en l'honneur de son dieu, parce qu'il avait livré à ses mains l'ennemi, celui qui faisait de la patrie un désert, et qui multipliait les morts parmi nous.
Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka mdani wathu mʼmanja mwathu, ndiye amene anawononga dziko lathu, napha anthu athu ambirimbiri.”
25 Lorsque leur cœur se fut ainsi réjoui, ils dirent: Faites venir Samson de la geôle, pour qu'il nous serve de jouet. L'on fit donc venir Samson de la maison du geôlier, et il leur servit de jouet; ils le souffletèrent, et ils le placèrent entre les colonnes.
Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi. Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati.
26 Et Samson dit au jeune homme qui le menait par la main: Fais-moi toucher les colonnes sur lesquelles repose le temple, et je m'y appuierai.
Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.”
27 Or, le temple était rempli d'hommes et de femmes; il y avait là tous les chefs des Philistins, et, sur la plate-forme, environ trois mille hommes et femmes, qui regardaient Samson et le jeu qu'on faisait de lui.
Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera.
28 Et Samson pleura devant le Seigneur, et il dit: Seigneur Adonaï, souvenez-vous de moi, et me rendez encore une fois mes forces, ô mon Dieul qu'une fois au moins je tire vengeance des Philistins, pour mes deux yeux.
Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.”
29 Et Samson saisit les deux colonnes du temple sur lesquelles reposait l'édifice et où il s'était appuyé; il en prit une de la main droite, l'autre de la main gauche;
Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso,
30 Et Samson dit: Mort à moi et aux Philistins! Puis, il ébranla les colonnes avec force; le temple s'écroula sur les chefs et sur le peuple qu'il contenait. Et Samson en mourant fit périr plus d'hommes qu'il n'en avait tué pendant sa vie.
ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.
31 Ses frères et la famille de son père vinrent le prendre. Et ils s'en retournèrent, et ils l'ensevelirent entre Saraa et Esthaol, dans le sépulcre de Manué son père. Or, il avait jugé Israël vingt ans.
Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.

< Juges 16 >