< Juges 15 >
1 Après cela, au temps de la moisson du froment, Samson partit avec un chevreau pour visiter sa femme, et il dit: Je veux entrer auprès de ma femme dans la chambre nuptiale; mais son beau-père ne lui permit pas d'entrer.
Patapita nthawi, mu nyengo yodula tirigu, Samsoni anatenga kamwana kambuzi ndipo anapita kukacheza kwa mkazi wake. Iye anati, “Ndikufuna kukalowa ku chipinda cha mkazi wanga.” Koma abambo a mkaziyo anamuletsa kutero.
2 Il le retint, disant: J'ai pensé que tu la haïssais, et je l'ai donnée à l'un de tes amis; n'a-t-elle pas une sœur plus belle et plus jeune? Qu'elle soit ta femme, au lieu de la première.
Abambo a mkaziyo anati, “Ine ndimaganiza kuti umamuda kwambiri nʼchifukwa chake ndinamupereka kwa mnzako. Kodi mngʼono wake uja sindiye wokongola kupambana iye? Ingotengani ameneyo mʼmalo mwake.”
3 Et Samson leur dit: Je suis irrépréhensible cette fois; je suis innocent, cette fois encore, à l'égard des Philistins, en leur faisant du mal.
Samsoni anawawuza kuti, “Pano sindikhala wochimwa ndikawachita choyipa chachikulu Afilistiwa.”
4 Et Samson s'en étant allé, prit trois cents renards et trois cents torches; il accoupla les renards côte à côte, et il attacha une torche entre deux queues;
Choncho Samsoni anapita nakagwira nkhandwe 300 nazimangirira michira ziwiriziwiri ndipo pa fundo iliyonse ya michirayo anamangirira nsakali.
5 Puis, il alluma les torches, et il lança les renards au milieu des blés des Philistins; les blés furent détruits depuis le sol jusqu'à l'épi, et la flamme atteignit les vignes et les oliviers.
Anayatsa nsakalizo kenaka ndi kuzitayira nkhandwe zija mʼminda ya tirigu ya Afilisti, ndipo zinatentha milu ya tirigu, ndi wosadula yemwe pamodzi ndi mitengo ya mpesa ndi ya olivi.
6 Les Philistins dirent: Qui a fait cela? Et on leur répondit: C'est Samson, l'époux de Thamni, parce que le père de celle-ci lui a pris sa femme et l'a donnée à l'un de ses amis. Et les Philistins partirent, et ils la livrèrent aux flammes, elle et la maison de son père.
Tsono Afilisti anayamba kufunsana kuti, “Ndani wachita izi?” Ena anati, “Ndi Samsoni mkamwini wa munthu wa ku Timna uja chifukwa Mtimunayo anatenga mkazi wake ndi kumupereka kwa mnzake.” Choncho Afilisti anapita kukatentha mtsikanayo pamodzi ndi abambo ake.
7 Et Samson dit: Puisque vous l'avez traitée de la sorte, certes, j'en tirerai vengeance sur vous, jusqu'à ce qu'il me plaise de cesser.
Samsoni anawawuza kuti, “Ngati mumachita zangati zimenezi, ndiye ine sindileka mpaka nditakulipsirani.”
8 Et il les frappa en les bouleversant; ce fut une plaie très-grande; ensuite, il alla s'établir dans le souterrain de la roche d'Etam.
Choncho Samsoni anamenyana nawo koopsa ndipo anapha ambiri a iwo. Kenaka anakalowa mʼphanga la Etamu, nakhala momwemo.
9 Les Philistins, s'étant mis en campagne, campèrent en Juda, et ils essuyèrent un échec au lieu dit la Mâchoire.
Pambuyo pake Afilisti anakamanga misasa ya nkhondo mʼdziko la Yuda, ndi kuthira nkhondo mʼdera la Lehi.
10 Et Juda leur dit: Pourquoi avez-vous marché contre nous? Ils répondirent: Nous sommes venus pour exterminer Samson et le traiter comme il nous a traités.
Anthu a fuko la Yuda anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwabwera kudzamenyana nafe?” Iwo anayankha kuti, “Tabwera kudzamanga Samsoni ndi kuti timuchite zofanana ndi zimene anatichita.”
11 Trois mille hommes de Juda descendirent alors a la caverne de la roche d'Etam, et ils dirent à Samson: Ne sais-tu pas que les Philistins nous dominent? Pourquoi donc nous as-tu amené cette affaire? Et Samson leur dit: Je les ai traités comme ils m'avaient traité.
Ndipo anthu 3,000 a ku Yuda anapita ku phanga la Etamu, ndi kukamufunsa Samsoni kuti, “Kodi iwe sudziwa kuti ife amatilamulira ndi Afilisti? Tsono ndi chiyani chimene watichitachi?” Iye anayankha kuti, “Ine ndinachita zomwe iwo anandichita.”
12 Et ils lui dirent: Nous sommes descendus pour te lier et te remettre en leurs mains. Et Samson leur dit: Jurez que vous-mêmes, vous n'êtes point venus contre moi?
Iwo anati kwa iye, “Ife tabwera kuti tikumange ndi kukupereka kwa Afilisti.” Ndipo Samsoni anati, “Lonjezani mwa lumbiro kuti simundipha ndinu.”
13 Ils lui répondirent: Nullement, mais nous allons te charger de liens pour te livrer à eux, et nous ne te tuerons pas. Ils le lièrent donc avec deux cordes neuves, et ils l'enlevèrent de cette roche.
Iwo anamuyankha kuti, “Ayi, ife sitikupha. Koma tingokumanga ndi kukupereka mʼmanja mwa Afilisti.” Choncho anamumanga ndi zingwe ziwiri zatsopano namutulutsa mʼphanga muja.
14 De là, ils allèrent jusqu'au lieu dit la Mâchoire, et les Philistins jetèrent de grands cris, et ils accoururent à sa rencontre. Aussitôt, l'Esprit du Seigneur s'élança sur lui, et les cordes qui lui retenaient les bras furent pour lui comme de l'étoupe brûlée, les liens de ses mains se rompirent.
Samsoni anafika ku Lehi, ndipo Afilisti anamuchingamira akufuwula. Nthawi yomweyo Mzimu wa Yehova unatsika pa iye mwamphamvu ndipo zingwe zimene anamumanga nazo zinasanduka ngati thonje lopsa mʼmoto, zinachita ngati zasungunuka nʼkuchoka mʼmanja mwake.
15 Et il trouva à terre une mâchoire d'âne, et il étendit la main, et il la ramassa, et, avec cette mâchoire, il tua mille hommes.
Anapeza chibwano cha bulu amene anali atangofa kumene. Anachitola ndi kuphera nacho anthu 1,000.
16 Et Samson dit: Avec une mâchoire d'âne, je les ai détruits, et je les ai détruits; avec une mâchoire d'âne, j'ai tué mille hommes.
Ndipo Samsoni anati, “Ndi chibwano cha bulu, milu ndi milu ya anthu. Ndi chibwano cha bulu, ndapha anthu 1,000.”
17 Lorsqu'il eut cessé de parler et qu'il eut jeté la mâchoire, il appela ce lieu l'Elévation de la Mâchoire.
Atatsiriza kuyankhula, anataya chibwanocho, ndipo malowo anawatcha Ramati-Lehi.
18 Il avait bien soif et il pleura devant le Seigneur, et il dit: Il vous a plu d'opérer cette grande délivrance par la main de votre serviteur; vais-je maintenant mourir de soif et retomber entre les mains des incirconcis?
Pambuyo pake anamva ludzu kwambiri ndipo anayitana Yehova mopempha kuti, “Inu mwapatsa mtumiki wanu chipulumutso chachikulu chotere. Kodi tsopano ndife ndi ludzu ndi kugwidwa ndi anthu osachita mdulidwewa?”
19 Et le Seigneur ouvrit le creux de la mâchoire, et de l'eau en jaillit, et Samson but, et il ranima ses esprits, et il revint à la vie. A cause de cela, on donna à cette source le nom de Fontaine de l'Invocation, et encore de nos jours elle existe au lieu dit la Mâchoire.
Pamenepo Mulungu anangʼamba nthaka ku Lehi, ndipo madzi anatuluka mʼdzenjemo. Samsoni anamwa madziwo, ndipo mphamvu zake zinabwerera nakhalanso monga analili. Choncho chitsimecho chinatchedwa Eni-Hakore, ndipo chilipobe ku Lehiko mpaka lero.
20 Or, Samson jugea vingt ans Israël aux jours des Philistins.
Samsoni anatsogolera Israeli pa nthawi ya Afilisti kwa zaka makumi awiri.