< Josué 5 >
1 Lorsque les rois des Amorrhéens de la rive droite du fleuve, et les rois des Phéniciens de la côte, apprirent que le Seigneur Dieu avait desséché le Jourdain devant les fils d'Israël pendant qu'ils le traversaient, leur intelligence fut paralysée, l'épouvante les saisit, et il ne leur resta pas ombre de prudence devant les fils d'Israël.
Mafumu onse a Aamori, a kummawa kwa Yorodani ndi mafumu onse a Akanaani a mʼmbali mwa Nyanja anamva momwe Yehova anawumitsira Yorodani pamene Aisraeli ankawoloka. Choncho anachita mantha ndi kutayiratu mtima chifukwa cha Aisraeliwo.
2 Vers ce temps-là, le Seigneur dit à Josué: Fais-toi des couteaux de pierre tranchante, convoque les fils d'Israël de la seconde génération, et soumets-les à la circoncision.
Tsono Yehova anati kwa Yoswa, “Panga mipeni ya miyala ndipo uchitenso mwambo wa mdulidwe pa Aisraeli.”
3 Et Josué fit des couteaux de pierre tranchante, et il circoncit les fils d'Israël, au lieu appelé: les collines des Prépuces.
Choncho Yoswa anapanga mipeni ya miyala ndi kuchita mdulidwe Aisraeli ku Gibeyati Haaraloti.
4 C'est ainsi que Josué purifia les fils d'Israël: tous ceux qui étaient nés dans le voyage, et tous ceux qui, à la sortie d'Egypte, n'avaient point été circoncis,
Chifukwa chimene Yoswa anachitira izi ndi ichi: Onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto, amuna onse amene anali oyenera kumenya nkhondo anatha kufa mʼchipululu atatuluka mʼdziko la Igupto.
5 Josué les circoncit tous;
Anthu onse amene anatuluka mʼdziko la Igupto anali atachita mwambo wa mdulidwe, koma onse amene anabadwira mʼchipululu, pa ulendo wochoka ku Igupto, sanachite.
6 Car, pendant quarante-deux ans, Israël avait erré dans le désert de Mabdaris. C'est pourquoi la plupart des hommes en état de porter les armes, qui, après la sortie d'Egypte, s'étaient montrés indociles aux ordres du Seigneur, n'avaient point été circoncis; aussi le Seigneur les avait-il condamnés à ne jamais voir la terre que le Seigneur avait juré de donner à leurs pères, terre où coulaient le lait et le miel.
Aisraeli anakhala akuyenda mʼchipululu kwa zaka makumi anayi mpaka amuna onse amene potuluka mʼdziko la Igupto anali a msinkhu woyenera kupita ku nkhondo anamwalira. Iwo anafa chifukwa sanamvere mawu a Yehova. Yehova anawalumbirira kuti sadzalowa konse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi limene analonjeza kwa makolo awo kuti adzatipatsa.
7 Et à ces hommes, le Seigneur substitua leurs fils, ceux que Josué circoncit, parce qu'ils étaient nés pendant le voyage, et n'avaient point été circoncis.
Koma ana awo amene analowa mʼmalo mwawo ndiwo amene Yoswa anawachita mdulidwe popeza sanachite pamene anali pa ulendo wawo mʼchipululu muja.
8 Après leur circoncision, ils se tinrent en repos et restèrent dans leur camp jusqu'à ce qu'ils fussent guéris.
Atamaliza kuchita mdulidwe uja, anthu onse anakakhala ku misasa yawo kudikira kuti zilonda zipole.
9 Et le Seigneur dit à Josué, fils de Nau: J'ai effacé aujourd'hui parmi vous l'opprobre d'Egypte, et le nom de Galgala fut donné à ce lieu.
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Kuyambira tsopano anthu a ku Igupto sadzakunyozaninso.” Nʼchifukwa chake malowa anatchedwa Giligala mpaka lero.
10 Ensuite, les fils d'Israël célébrèrent la pâque le quatorzième jour de la lune, après le coucher du soleil, à l'Occident de Jéricho, sur la rive du Jourdain, dans la plaine.
Akupumulabe ku Giligala kuja mʼchigwa cha Yeriko, Aisraeli anachita chikondwerero cha Paska madzulo pa tsiku la 14 la mwezi woyamba womwewo.
11 Ils mangèrent des azymes faits du blé nouveau de cette terre.
Mmawa mwake ndi pamene anayamba kudya zakudya za mʼdziko la Kanaani. Anaphika buledi wopanda yisiti ndi kukazinga tirigu tsiku lomwelo.
12 Ce jour-là, il n'y eut plus de manne; dès que les fils d'Israël eurent mangé du grain de cette terre, la manne cessa de tomber pour eux. Ils récoltèrent dans cette année les fruits de la terre des Phéniciens.
Atangodya chakudya cha mʼdzikomo, mana anasiya kugwa, ndipo sanapezekenso. Kuyambira nthawi imeneyo Aisraeli anayamba kudya chakudya cha mʼdziko la Kanaani.
13 Et comme Josué était dans le pays de Jéricho, voilà que, levant les yeux, il vit devant lui un homme debout, une épée nue à la main. Et Josué l'abordant, lui dit: Es-tu des nôtres, ou de nos ennemis?
Tsiku lina pamene Yoswa anali pafupi ndi Yeriko, anakweza maso ake ndipo mwadzidzidzi anaona munthu atayima patsogolo pake ndi lupanga losolola mʼdzanja lake. Yoswa anapita pamene panali munthuyo ndipo anamufunsa kuti, “Kodi uli mbali yathu kapena ya adani athu?”
14 Et l'homme lui répondit: Je suis le prince de la milice du Seigneur, et je suis venu maintenant près de toi. A ces mots, Josué tomba la face contre terre, et dit: Maître, que commandes-tu à ton serviteur?
Iye anayankha kuti “Sindili mbali iliyonse. Ndabwera monga mkulu wa asilikali a Yehova.” Pomwepo Yoswa anadzigwetsa chafufumimba kupereka ulemu, ndipo anamufunsa, “Kodi mbuye wanga muli ndi uthenga wotani kwa mtumiki wanu?”
15 L'archange du Seigneur reprit: Ote la chaussure de tes pieds, car le lieu où tu les poses est saint.
Mkulu wa asilikali a Yehova uja anayankha kuti, “Vula nsapato zako, pakuti wayima pa malo wopatulika.” Ndipo Yoswa anachitadi zimene anawuzidwazo.